Return   Facebook

The Universal House of Justice

Ridván 2018

To the Bahá’ís of the World

Dearly loved Friends,

Tikukulonjerani mu kuwala kwa nyengo zosayiwalika zomwe zimapanga chikondwelero cha zaka 200 za kubadwa kwa Wokongola Wodalitsikayo. Pomwe tikuganizira zomwe zinachitika nthawi iyi komanso kuyambira pamenepa, tikupeza kuti mbumba yachiBaha'i ya dziko lonse yapano silinso chimodzi-modzi ndi pomwe imayamba paulendo wake ma sayiko asanu ndi imodzi a Pulani yapanoyi. Ili yokhudzika kuposa mmbuyomu ndi ntchito yake. Yaonetsa kuvumbulutsika kwakulu pa kuthekera kwake kubweretsa abwenzi ndi ogwira nawo ntchito limodzi mu mngwirizano ndi moyo wa mbumba; kutsogolera madera ndi midzi mu ntchito yogwirizana; kukambirana momwe zoonadi zauzimu zingamasulilidwe mu ntchito yopitilira; komanso, kupitilira apo; kukambirana osati za ziphunzitso zomwe zingamange dziko latsopano kokha, komanso zokhudza Iye Amene adaphunzitsa izo: Baha’u’llah. Nkhani za moyo Wake ndi kuzunzidwa Kwake zokambidwa ndi malilime ochuluka a akulu, achinyamata ndinso ana zinakhudza mitima yosawerengeka. Ena anadziwonetsa okha kuti akonzeka kufufuza Chipembedzo Chake mopitilira. Ena analonjeza kutenga nawo mbali. Ndipo mizimu yambiri yomasuka inasunthidwa kutsimikizira ku chikhulupiliro chawo.

Chimodzi mwa zoonetsa zonenedwa za kupita patsogolo kunali malo ochuluka komwe kunaonekeratu kuti Chipembedzo chadzuka kuchokera ku kusadziwika mu mdziko. Panali atsogoleri a boma and atsogoleri ena amene ananena poyera – ndiponso nthawi zina kutsindika mwapadera- kuti dziko likufunika masomphenya a Baha’u’llah ndipo kuti ntchito za aBaha’i ndi zosililika ndipo zikuzidwe. Chinatikondweretsa ife kuona kuti si aBaha’i okha amene anafuna kulemekeza Baha’u’llah ndi kukondwelera moyo Wake – kusonkhana kwapadera kunachitika ndi ena osakhala aBaha’i. M’madera momwe muli kusagwirizana ndi Chipembedzo, abwenzi sanaope, iwo anaonetsa kumasuka kodabwitsa, analimbikitsa amnzawo kufufuza choonadi mwa iwo okha, ndipo ambiri anatenga nawo mbali pa zikondwelero mosangalala. Chikondwelera cha zaka 200 zakubadwa kwa Baha'u'llah kunapangitsa kudzuka kwa maluso osiyana-siyana a zisangalaro, umboni waukulu wa kasupe wa chikondi momwe unachokera. Khalidwe la mbumba yachiBaha’i ku kapangidwe ka chikondwelero ichi linali momwe zambiri zaphunziridwira kwa zaka zoposa makumi awiri tsopano, chiyambireni mndandanda wapano wa mapulani a zaka zisanu. Wokhulupilira payekha anatengapo mbali, mbumba inadzuka kugwira ntchito limodzi, ndipo abwenzi analunjikitsa mphamvu zawo ku mapulani okonzedwa ndi zikhadzikitso. Chikondwelero chopatulika, kukwaniritsa kudutsa kwa zaka zikwi ziwiri, zopereka kudzuka kwa mphamvu kwambiri ku ntchito yomanga mbumba ku zaka zina chikwi zili mkubwera. Munyengo yotsogozana ndi chikondwelero china cha zaka 200 chachiwiri, lolani mbeu iliyonse yodzalidwa ndi chikondi pa chikondwelero choyamba ileledwe modekha kuti ipereke zipatso.

Zaka ziwiri mu Pulani yapano, ngakhale kuti kupita patsogolo mosakakamiza sikungakhale kofanana mdziko lililonse, chiwerengero cha mapologalamu a kukula a kathithi padziko lonse chikuyandikira theka la nambala ya 5000 yomwe inayikizidwa mu ntchito za pulani yapanoyi, ndipo mlingo umene nambalayi ikukwelera wakhala ukukula. Kuyang’anitsitsa mchifupi, pali zizindikiro zolonjeza za momwe mphamvu ndi kuthekera kwa anthu, mbumba ndi zikhadzikitso zikuonekera. Kwa okhulupilira kulikonse, kuphunzira kwa zaka 200 za chikondwelero komwe kunaonetsera kuti kukambirana kwawo kwa tsiku ndi tsiku ndi anthu owazungulira kukhoza kulumikizitsidwa ndiuzimu wa kuphunzitsa. Ndipo pomwe ntchito mmidzi mazana-mazana ndi mmadera ikupita patsogolo, moyo wokhadzikika wa mbumba ukukhadzikika monsemo. Chiwerengero cha makalasita komwe ndondomeko yokulitsa patani ya zochita ku madera ochuluka ikukhadzikika bwino lomwe – kulora, chomwecho, abwenzi kudutsa mtunda wachitatu pa mndandanda wa kukula chapita patsogolo kwambiri. Ndi apa, pamalo ophunzirira aBaha’i padziko lonse, makamaka poyendetsa miyanda-miyanda ya anthu ku masomphenya a Baha'u'llah, kumene osati chiwerengero chachikulu chikubwera kutenga nawo mbali mu zochita-chita za aBaha’i komanso abwenzi tsopano akuphunzira momwe magulu ang’ono-angóno akuzizindikiritsa okha ndi mbumba ya Dzina Lalikulu Kwambiri. Tikuona kuyesetsa pa maphunziro a Chipembedzo akuyamba kutenga chikhazikiko chabwino mmalo amenewa, pomwe ana akuyenda mosajejema mu mndandanda wa maphunziro chaka ndi chaka komanso mlingo umodzi wa maphunziro auzimu a achinyamata achisodzera ukusuntha kufika pa mlingo wina. Mmalo amenewa, insitichuti zikuphunzira kuonesetsa kuti anthu okwanira otumikira akusulidwa kuti athe kupereka maphunziro auzimu ndi chikhalidwe cha ana ndi achinyamata achisodzera omwe chiwerengero chawo chikukulira-kulira. Kutenga mbali mu zochita-chita izi zomanga maziko mwa ana kukuyamba kukhadzikika mzikhalidwe za unyinji omwe umaonedwa monga mbali imodzi yofunika ya moyo wa mbumba. Nyonga zatsopano zikuyamba kutuluka mwa anthu omwe akutenga chitsogolo cha chitukuko chawo chomwe, ndipo akumanga chitetezo ku mphamvu zam’dera zomwe zimabweretsa maganizo osemphana. Kuthekera kwa kupita patsogolo kwa kuthupi ndikuuzimu kukuoneka. Uweniweni wadera wayamba kusintha.

Abwenzi okondedwa, iyi ndithudi ndi nthawi yopereka mathokozo kwa Wokondedwa Wabwino. Pali zifukwa zambiri zazikulu zolimbikitsa. Komabe tikuzindikira bwino lomwe za kukula kwa ntchito yomwe yatsalira. Chofunikira, momwe tidanenera mmbuyomu, kuyenera kuonekera mma kalasita ochuluka gulu lopitilira la okhulupilira amene angathe, ndi ena owazungulira, kupitiliza ntchito yokulitsa ndi kumanga kuthekera, ndi amene angasiyanitsidwe kamba ka kuthekera kwawo ndi khalidwe kuunikira pa ntchito ndi kuphunzira kudzera mu kuchita. Kukulitsa ndi kuyendera limodzi ndi gulu la anthu mmalo aliwonse – osati mkalasita mokha komanso mmadera ndi mmidzi – ndi ntchito yovuta koma yofunika kwambiri. Koma komwe izi zikuchitika, zotsatira zikuchitira umboni.

Ndife achikhulupiliro kuona kuti zikhadzikitso za Chipembedzo zikusunga kufunika uku kwakukulu patsogolo pa maganizo awo, kupeza njira zabwino zothandizira kuphunzira kochokera mu kupita patsogolo kuti kugwire ntchito mmadera ambiri. Panthawi yomweyo, kuphunzira kwakukulu kukupereka ku zikhadzikitso za mdziko, mzigawo,ndi mmadera masomphenya aakulu. Zayamba kukhudzidwa m’mbali zonse za chitukuko cha mbumba ndipo ndi okhudzidwa ndi ubwino wa anthu osati mamembala ake okha. Pozindikira zovuta zokhadzikika zomwe ndondomeko ya insitichuti ili nazo pa kutukuka kwa anthu, zikupereka chidwi chachikulu pa momwe ma insitichuti angalimbitsidwe. Zikukhala okhudzika pa kufunika kolimbitsa chidwi cha mbumba pa zofunika za Pulani ndi kuyitanira gulu la abwenzi lokulira-kulira ku milingo yayitali ya umodzi. Zikukweza mokhulupirika udindo wawo kukonza bwino ndondomeko zawo za kayendetsedwe ndi zachuma kuti ntchito ya kukula ndi kulimbitsa ithandizidwe bwino. Mu zonse izi, zikukhala zotanganidwa ndi kupeza mu mbumba zoyenelera zomwe zingapangitse kutulutsa mphamvu zauzimu.

Pomwe ntchito ya kumanga mbumba ikukula, abwenzi akugwiritsa ntchito kuthekera kwatsopano komwe apeza kusintha kakhalidwe ka mdera lowazungulira, mphamvu zawo zayasidwa kamba ka kuphunzira kwa ziphunzitso zoyera. Ntchito za kanthawi pang’ono nazonso zakwera mchiwerengero, ntchito za ndondomeko nazo zakulanso, ndipo tsopano kuli zitukuko zochuluka zachiBaha’i zomwe zikugwira ntchito ya maphunziro, umoyo, zaulimi ndi mbali zina. Kuchokera mu zotsatira za kusinthika zoonekeratu mwa munthu komanso mmiyoyo pamodzi ya anthu ikusiyanitsa zoyambitsa zosasokonekera za mphamvu yomanga dera ya Chipembedzo cha Baha’u’llah. Nchifukwa chake, tsono, kuchokera mu zochitika izi za ntchito za mdera – zophweka kapena zolimba, za nthawi yayifupi kapena yayitali – maofesi oona za Mbumba yachiBaha’i ya Kunja (Baha’i International Community) akupeza chilimbikitso mopitilira mu kuthekera kwawo kutenga mbali mu ntchito zosiyana-siyana za dera. Iyi ndi mbali imodzi ya ntchito ya Chipembedzo imene yachita bwino. Pa mlingo wa dziko, zosonkhera ku ntchito zomwe zili za tanthauzo mdera – kufanana kwa amuna ndi akazi, maulendo ndi kuchitira limodzi, udindo wa achinyamata pa kusinthika kwa ntchito za chitukuko, ndi kulolerana kwa Zipembedzo, kungotchulapo zina – zikupangidwa ndi kudzikhulupilira kwakukulu, luso, ndi kuzindikira. Ndipo kulikonse komwe akukhala, kugwira ntchito, kapena kuphunzira, okhulupilira a misinkhu yonse ndi mitundu yonse akusonkhera kwakukulu ku ntchito zina zofunikira, kubweretsa kuzindikira kwa iwo amene awazungulira iwo njira yabwino yowumbidwa ndi Chibvumbulutso chachikulu cha Baha'u'llah.

Kukhadzikika kwa Chipembedzo mmalo osiyana-siyana momwe ntchito ikutambasuka kwakhala kukupita patsogolo ndi kupezeka kwake pa makina a intaneti a dziko lonse, kupezeka komwe kwakula kwambiri kudzera mu kukhadzikitsa kwama webusayiti ochuluka achiBaha’i ndi kukuza kwa masayiti ena pa Baha'i.org. Izi zili ndi ubwino waukulu ku ntchito ya kufalitsa ndi kuteteza Chipembedzo. Kwa masiku ochepa okha gulu la anthu lochuluka linakopeka ku zolemba zosamala bwino zokhudza Chipembedzo zomwe zinayikidwa pa webusayiti ya chikondwelero cha zaka 200 zomwe zinayikidwa mzinenero zisanu ndi zinai, ndipo tsopano zakuzidwa mmaiko paokha-paokha kufotokoza kusakanikirana kwa zikondwelero zomwe zinachitika. Mapulani ali kale mkati kuti kukhadzikitsidwe webusayiti yosungirako uthenga (Reference Library) yachiBaha’i, chipangizo chimene chipereke mwayi ku ma Tabuleti osamasulilidwa ndi kusindikizidwa a mMalembo Oyera kuti atulutsidwe pamenepo. Pamwamba pa izi, mabuku a Zolemba za Baha'ú'llah ndi Abdu’l-Baha zomwe zayikidwa mchingerezi tsopano zioneka mzaka zikubwerazi.

Ku Santiago, Chile ndi Battambang, Cambodia, Nyumba Zopembedzeramo zatsopano padziko lonse zikuyamba kukhala malo achikoka, zizindikiro za chimene Chipembedzo chikuyimira. Ndipo chiwerengero chawo chikula posachedwa. Ndife okondwa kulengeza kuti mwambo woyikiza Nyumba Yopembedzera yaku Colombia, Norte del Cauca, udzachitika mwezi wa Julaye. Kupitiliza apo, kumanga kwa Nyumba Zopembedzera zoonjezera kuli chifupi. Ku Vanuatu, ntchito yotenga chilolezo ili mkati kuti Nyumbayi iyambe kumangidwa. Ku India ndinso ku DR Congo, ndondomeko yayikulu ndi yokhwima tsopano yamalizidwa yomwe yathandiza kupeza malo oti padzamangidwe Nyumbazi. Chisangalaro poona ndondomeko ya kamangidwe ka Mashiriku-Adhkar yoyamba ku Papua New Guinea pa Naw-ruz kunafika pamodzi ndi kuwulutsa ndondomeko ya momwe Nyumba Yopembedzera yamdera idzamangidwire ku Kenya. Pakadali pano, tili ndi chiyembekezo kuti mauthenga omwe anatulutsidwa posachedwa okhudza chikhadzikitso cha Mashriku-Adhkar, okonzedwa ndi Nthambi yathu ya Kafukufuku, apitiliza kupanga abwenzi kuyamikira kufunika kwa kupembedza pa moyo wa mbumba. Pakuti mu ntchito zawo zakutumikira, makamaka, mmisonkhano yawo ya mapemphero, aBaha'í kulikonse akuyika maziko auzimu a Nyumba Zopembedzera za mtsogolo.

Tsopano kwatsala zaka zitatu zokha za ntchito ya kota ya zaka theka la chikwi yomwe inayamba mchaka cha 1996 yomwe imalunjika kwambiri pa golo limodzi: kupititsa patsogolo kulowa mwaunyinji. Pa Rizwani 2021, otsatira a Baha'ú'llah adzayamba Pulani ya chaka chimodzi. Yayifupi, koma yodzadza ndi chenjezo, ntchito iyi ya chaka chimodzi idzayambitsa funde latsopano la Mapulani onyamula chombo cha Chipembedzo kupita ku zaka 100 za ndime yachitatu yachi Baha'í. Mu miyezi imeneyi khumi ndi iwiri, kukumbukira kwa dziko lachi Baha'í kwa zaka 200 za kukwera kumwamba kwa Abdu’l-Baha kuzaphatikizapo mwa zina msonkhano ku Likulu la aBaha'í komwe oyimira a Mabungwe Auzimu a Mmaiko ndi makhonsolo onse adzayitanidwa. Ichi, komabe, chidzakhala chinthu choyambilira mu mndandanda wa zochitika zomwe zidzakonzekeretsa okhulupilira ku ntchito ya zaka za mtsogolo. M’mwezi wa januwale chaka chotsatira, kukwaniritsa zaka 100 chiwerengereni poyera Chifuniro cha Abdu’l-Baha idzakhala nthawi ya msonkhano waukulu ku Malo Oyera kubweretsa pamodzi Alangizi ndi Athandizi awo a kuteteza ndi kufalitsa. Mphamvu zauzimu zomwe zidzatulutsidwe ku misonkhano imeneyi mu mbiri ya Chipembedzo zidzayenera kufikira kwa abwenzi onse a Mulungu ku mbali iliyonse ya dziko yomwe akukhala. Pa chifukwa ichi, mndandanda wa misonkhano udzachitika mmiyezi yotsatira, yotsogolera ku ntchito ya zaka zochuluka zomwe zidzatsatira pamapeto pa Pulani ya Chaka Chimodzi.

Ndime yatsopano ya kutambasuka kwa Pulani Yoyera ya Abdu’l-Baha ikubwera. Koma masomphenya osangalatsa ndi a posachedwa ali patsogolo pathu. Chikondwelero cha zaka 200 za kubadwa kwa Bab chili pafupi, chaka ndi theka zikubwerazi. Iyi ndi nyengo yokumbukira kudzipereka molimba mtima kwa Martyr-Herald (Mkupamame wa a Maritiri) wa Chipembedzo chathu, Yemwe ntchito yake yodzadza ndi zotchinga inakankhira mtundu wa anthu ku ndime yatsopano ya mbiri. Ngakhale ikusiyanitsidwa ndi zaka pafupi zikwi ziwiri ndi nthawi yathu ino, mbumba yomwe Bab anaonekera ikufanana ndi dziko la lero chifukwa cha kuponderezana ndi kufunitsitsa kwa anthu ochuluka kupeza mayankho okwaniritsa ludzu la mzimu lofuna kudziwa. Poganizira za momwe zisangalaro za zaka 200 izi zidzakhalire, tikuzindikira kuti zikondwelero zimene zidzakhala zapadera-dera. Komabe, tikuyembekezera zochita-chita zosachepera zochuluka ndi zozadza monga momwe zinalili pa zikondwelero 200 zapita. Ndi mwambo umene mbumba iliyonse, nyumba iliyonse, mtima uliwonse mosakayika udzayangánirako ndi chiyembekezo.

Miyezi iwiri yotsatira idzakhalanso nthawi yokumbukira miyoyo ya omtsatira a Bab olimba mtima – (heroes and heroines) amene chikhulupiliro chawo chinaonetsedwa mu ntchito za kudzikhuthula kosafanizirika kumene kudzakongoletsa mbiri ya Chipembedzo. Makhalidwe awo opanda mantha, kudzipereka, ndi kudzipatula ku zilizonse koma Mulungu kukhudza iwo okha pa aliyense amene adamva za ntchito zawo. Ndi zokhudza bwanji, indedi, msinkhu wawo wachichepere pomwe ambiri olimba mtimawa anasiya chizindikiro chosayiwalika ku mbiri. Mu nthawi ikubwerayi, chitsanzo chawo chipereke kulimba mtima ku gulu lonse la okhulupilira – maka achinyamata, amene akuyitanidwanso kutsogolera ntchito yomwe cholinga chake ndi kusintha dziko lapansi.

Ichi, tsono, ndi chikhulupiliro chathu chowalitsitsa. Mu masayiko asanu ndi imodzi amene ali mu Rizwani yapano kufikira chikondwelero cha zaka 200 za Bab zikubwerazi – indedi, mu zaka zitatu zotsalazi pofika mapeto a Pulani ino – lolani chikondi chomwecho chomiza ndi chopatulika chomwe chinalimbikitsa omsatira a Bab kugawa kuwala koyera kukulimbikitseni inu ku ntchito zazikulu. Kuti inu mukhale zolandiriramo za thandizo la kumwamba, ndi pemphero lathu ku Malo Oyera.

 

Windows / Mac