Return   Facebook

The Universal House of Justice

Ridván 2019

To the Bahá’ís of the World

Dearly loved Friends,

Pomwe Chikondwelero Chachikulu Kwambiri chayandikira, tadzazidwa ndi mathokozo ndi chiyembekezo—kuthokoza pa zodabwitsa zimene Bahá’u’lláh wathandizira omutsatira Ake kukwanilitsa, chiyembekezo pa zomwe zili mtsogolo.

Mphamvu zomwe zinapezeka pa chikondwelero cha dziko lonse cha zaka 200 za kubadwa kwa Bahá’u’lláh zangopitilira kukula. Kupita patsogolo mofulumira kwa mbumba yachiBaha’i, kukwera kwa kuthekera kwake, ndi kutha kutapa mphamvu kuchokera mwa ambiri a mamembala ake kukuonekeratu kuchokera muzikwanilitso zaposachedwapa za dziko lonse. Mwa izi, kuchuluka kwa zochita-chita zomanga mbumba makamaka ndi zimene zaonekera kwambiri. Pulani za Zaka Zisanu yapano ikutsatira zaka makumi awiri za kuyesetsa kwa dziko lachiBaha’i kukonza ndi kuchulukitsa zochitikazi mwadongosolo— koma choyamikika, mu zaka ziwiri ndi theka za Pulaniyi, chiwerengero cha zochitikachitika pazokha chakwera kudutsa theka. Mbumba ya dziko lonse yaonetsa kuthekera kobweretsa anthu, nthawi ina iliyonse opitilira miliyoni mu zochita-chita zotere, kuwathandiza iwo kufufuza ndi kuvomera ku zoonadi zauzimu. Mu nyengo yayifupi yomweyi, misonkhano ya mapemphero nayo yawonjezereka pafupi-fupi kawili-yankho lofunikira kwambiri ku chibalaliko cha mtundu wa anthu chimene chikukulira-kulira ku Kasupe wa chiyembekezo ndi madalitso. Kupita patsogolo uku kwatenga lonjezo lapadera, pakuti misonkhano ya mapemphero imabweretsa mzimu watsopano mu moyo wa mbumba. Molukana ndi kuyesetsa kwa maphunziro a anthu onse, imalimbitsa cholinga chauzimu cha kuyesetsa kumeneku: kukulitsa mbumba zodziwika ndi chikondi chawo cha Mulungu ndi kutumikira kwawo ku mtundu wa anthu. Kulibenso kwina koma izi zaonekeratu koposa mma kalasita amenewa momwe kutenga mbali kwa chiwerengero chochuluka mu zochita-chita zachi Bahá’í zikupitilira mosalekeza ndipo abwenzi adutsa mtunda wachitatu pa kupita patsogolo kwa mbumba zawo. Ndife okondwa kuona kuti chiwerengero cha makalasita komwe ndondomeko ya kukula yapita patsogolo kufika apa yachulukanso kuposera theka chiyambireni cha Pulani ndipo pano chiwerengero chafika pa 500.

Kafuku-fuku uyu wachidule sangapereke chithuzi cheni cheni ku makulidwe a kusinthika komwe kukuchitika. Maonekedwe a zaka ziwiri zomwe zatsala za Pulani ndi owala. Zambiri zakwanilitsidwa mu chaka chathachi popereka maphunziro mokwanira ophunzilidwa kuchokera ku mapologalamu amphamvu a kukula mma kalasita amene monga timayembekezera, kuti akhale nkhokwe za kuphunzilira ndi zipangizo.Sentala Yayikulu ya Kuphunzitsa (ITC), ma khansala, ndi owathandizira awo sanalekeze poonesetsa kuti abwenzi m’mbali zonse za dziko atha kupindula kuchokera kufulumiza pa kuphunzira ndi kugwiritsa ntchito zophunziridwa zomwe zikupezeka mu makalasita awo. Tili osangalala kuona kuti mma kalasita ochuluka, komanso m’madera ndi m’midzi owazungulira, gulu la abwenzi latuluka amene kudzera mu ntchito zawo ndi kauni-uni akupeza zomwe zikufunikira, kuti ndondomeko ya kukula ipitilire patsogolo mmadera owazungulira. Akugwiritsa ntchito chida chothekera cha maphunziro a insitichuti, momwe kuthekera kosonkhera ku chitukuko chauzimu ndi kuthupi kwa mbumba kukupita patsogolo, ndipo pomwe akugwira ntchito, chiwerengero cha iwo amene akuwatsatira chikukula. Ndi chachidziwikire, madera ndi osiyana-siyana, ngakhalenso makulidwe. Koma kudzera mu kuyesetsa kwa dongosolo, aliyense akhoza kusonkhera mochilimika ku ntchito yomwe ilipo. Pamalo alionse, pali chisangalaro changwiro pochita kukambirana kwa tanthauzo ndi kolimbikitsa ndi mizimu ina, komwe kumabweretsa, mwachangu kapena mwapang’ono-pang’ono, kusunthika muuzimu. Pamene kuwala kwa lawi lomwe layatsidwa mumtima mwa wokhulupilira kuwalira-walira, mphamvu ya chikoka mwa iwo amene akhuzidwa ndi kutentha kwake nayonso imakula. Ndipo kwa mtima umene wamizidwa ndi chikondi cha Bahá’u’lláh, ndi chitinso chinthu china chofunikira koposa kufuna-funa mizimu yofanana nayo, kuwalimbikitsa pamene akulowa panjira ya kutumikira, kuyendera nawo limodzi pomwe akuphunzira ndi-mwinanso chisangalaro chachikulu pa zonse- kuona mizimu itatsimikizika mu chikhulupiliro chawo, kudzuka payokha, ndikuthandiza ena pa ulendo womwewu. Izi ndi zina mwa nyengo zapamwamba kwambiri zomwe moyo uwu waufupi ungakwaniritse.

Masomphenya opititsa patsogolo ntchito iyi yauzimu apangidwa osangalatsa ndi kuyandikira kwa chikondwelero cha zaka 200 za kubadwa kwa Báb. Monga chikondwelero chomwe chinapita, ichi ndi chikondwelero chopambana kwambiri. Chikupereka kwa aBahá’í onse Mwayi waukulu wodzutsa iwo amene awazungulira ku Tsiku la Mulungu lalikulu, ku kusefukira kodabwitsa kwa chisomo cha kumwamba kovumbulutsidwa ndi kuonekera kwa Abvumbulutsi awiri Oyera, Nyenyezi zotsatana Zomwe zinawalitsa dziko lonse lapansi. Muyeso wa zimene zikhoza kutheka mu ma sayiko awiri akubwerawa ndi wodziwika kwa onse kuchokera mu kuphunzira kochokera ku chikondwelero za zaka 200 za kubadwa kwa Baha’u’llah chomwe chinachitika zaka ziwiri zapitazo, ndipo zonse zimene zidaphunziridwa panthawi imene ija ziyenera zigwiritsidwe ntchito pa mapulani a zikondwelero za Aneneri Oyera Amapasa chaka chino. Pomwe chikondwelero cha zaka 200 za kubadwa kwa Bab kukuyandikira, tipemphera mosalekeza mmalo mwanu ku Manda Oyera, kupemphera kuti kuyesetsa kwanu kudzapereka ulemu waukulu kwa Bab kudzapambane kupititsa patsogolo Chipembedzo chomwe Iye analosera.

Kutsekera kwa zaka 100 za Nyengo Yomanga kwangotsalira zaka ziwiri ndi theka. Kudzakwanilitsa zaka 100 za kuyesetsa koyera kulimbitsa ndi kukulitsa maziko amene anayikidwa modzikhuthula mu Nyengo ya Kulimbatima ya Chipembedzo (Faith’s Heroic Age). Pa nthawi yomweyi mbumba yachiBaha’i idzakumbukiranso zaka 100 za kukwera kumwamba kwa ‘Abdu’l-Bahá, nthawi imene Mbuye wokondedwa anamasulidwa mu dziko ili ndi kukakhalanso ndi Bambo Ake mu ulemelero wosatha. Maliro Ake, amene anachitika tsiku lotsatira, anali chochitika “chimene Palesitina anali asanachioneko” Ku mapeto kwake, thupi Lake linayikidwa mu chipinda cha Manda a Bab. Komabe, kunaloseredwa ndi Shoghi Effendi kuti umu ndimongoyembekezera. Manda oyenera chikhalidwe ndi udindo wapamwamba wa Abdu’l-Baha adzayenera kumangidwa nyengo yoyenera ikadzafika.

Nthawi imeneyi yafika. Dziko lachiBaha’i likumemedwa kumanga nyumba imene idzasunga thupi loyeralo mpaka muyaya. Nyumba imeneyi imangidwe mkati mwa munda wa Rizwani, pamalo omwe mapazi a Wokongola Wodalitsika anayeretsapo; Manda a Abd’ul-Baha adzakhala pakati pa Manda Woyera ku Akka ndi Haifa. Ntchito yopanga chifani-fani cha nyumbayi ili mkati, ndipo zambiri zidziwika mmiyezi ikubwerayi. Chimwemwe chosaneneka chikusefukira mkati mwathu, pomwe tikuganizira za chaka chikubwerachi ndi zonse zimene chikulonjeza. Tikuyang’anira kwa wina aliyense wa inuiwo amene ali pa kaliki-liki kutumikira Bahá’u’lláh, kugwira ntchito mu dziko lililonse yobweretsa mtendere-kukwanilitsa kuyitanidwa kwanu kwapamwamba.

 

Windows / Mac