Return   Facebook

The Universal House of Justice

Ridván 2021

To the Bahá’ís of the World

Dearly loved Friends,

1. Mawu omaliza mu ndime yosayiwalika mu mbiri ya Chipembedzo tsopano alembedwa, ndipo tsamba latsegulidwa. Rizwani iyi ikukwaniritsa kumalizitsa kwa chaka chamtengo wapatali, cha Pulani ya Zaka Zisanu, ndi mndandanda wonse wa Pulani omwe unayamba mu chaka cha 1996. Mndandanda watsopano wa Mapulani ukukodola, ndi miyezi khumi ndi iwiri yomwe itumikire ngati mkupamame wa Pulani ya Zaka Zisanu ndi Zinayi (9) yomwe iyambe Rizwani yotsatira. Tikuona patsogolo pathu mbumba yomwe yapeza mphamvu mofulumira ndipo ndi yokonzeka kupita patsogolo. Koma pasakhale kunamizana pa momwe kuyesetsa kwakulu kunafunikira kuti tifike pamenepa ndi momwe zophunziridwa zinapezekera movutikira mkati mwa ndime: maphunziro omwe apezeka adzaumba tsogolo la mbumba, ndipo nkhani zamomwe adaphunzilira kukupereka chithuzi-thuzi cha zomwe zikubwera.

2. Zaka zochuluka kufikira 1996, zozadza ndi kupita patsogolo ndi kuphunzira kwapaokha, kunatsimikizira kuti chiwerengero chachikulu cha anthu mmadera ambiri chikhala chokonzeka kulowa mu Chipembedzo. Komabe, ngakhale chiwerengero chachikulu cha anthu olowa chinali cholimbikitsa chotere, sichinagwirizane ndi ndondomeko ya kukula yopitilira yomwe ikanapezeka mmalo osiyana-siyana. Mbumba inakumana ndi mafunso ozama amene, panthawi imeneyo, panalibe upangiri okwanira kuwayankha molondola. Kuyesetsa komwe cholinga chake chinali kukulitsa kukanapitilira bwanji mbali ndi mbali ndi ndondomeko ya kulimbitsa ndi kukonza zotchinga zapakanthawi ndi zooneka zovuta za kupititsa patsogolo kukula? Kodi anthu, zikhadzikitso ndi mbumba zikanadzutsidwa bwanji zokhala ndi kuthekera kotanthauzira ziphunzitso za Bahá’u’lláh mu ntchito? Ndipo kodi iwo amene anakopeka ndi ziphunzitso akanakhala bwanji otenga mbali mu ntchito yauzimu yadziko lonse?

3. Zinali chonchi kuti, theka la theka ya zaka 100 zapitazo, mbumba ya chi Bahá’í yomwe imatha kuwerengera Manja a Chipembedzo cha Mulungu atatu kutsogolo kwake inayamba ulendo wa Pulani ya Zaka Zinayi, yosiyana ndi mapulani omwe anabwera m’mbuyomo potsindika pa cholinga chimodzi: kupita patsogolo kwakulu pa ndondomeko yolowa mwaunyinji. Cholinga ichi chinafotokozera mndandanda wa Mapulani omwe anatsatira. Mbumba inali itamvetsetsa kale kuti ndondomeko iyi sinali kulowa mu Chipembedzo kwa magulu ocheperapo, kapena kuti iyamba payokha-yokha; zimatanthauza kukulitsa ndi kulimbitsa kwa cholinga, kwadongosolo ndi kofulumira. Ntchito iyi idzafunika kutenga mbali kodziwitsidwa bwino kwa mizimu yaochuluka, ndipo mu 1996, dziko la chiBahá’í lidamemedwa ku ntchito yayikulu yakuphunzitsa. Inayitanidwa kuti ikhadzikitse kulumikizana kwa ma insitichuti osulira anthu olunjika popeza chiwerengero chochuluka cha anthu odzozedwa ndi maluso ofunikira opititsa patsogolo ndondomeko ya kukula.

4. Abwenzi anayiyamba ntchitoyi ndi kuzindikira koti, poyang’anira zipambano zawo zam’mbuyo mu ntchito ya kuphunzitsa, makamaka anayenera kuphunzira za maluso amene amayenera kupeza ndiponso, kwakulu, momwe angawapezere malusowo. Munjira zambiri, mbumba zimatha kuphunzira pochita, ndipo maphunziro omwe imaphunzira, pomwe anasefeka ndi kukonzedwa powagwiritsa ntchito mmalo osiyana-siyana popita nthawi, adzayikidwa mu zipangizo zophunzilira. Panaoneka kuti zochita-chita zina zinali yankho lopezekeratu ku zofunikira zauzimu za unyinji. Masitade seko, makalasi a ana, mapemphero apamodzi, ndipo kenako magulu a achinyamata achisodzera zinaoeneka kufunika kwambiri kumbali iyi, ndipo pomwe zibweretsedwa pamodzi ndi zochitika-chitika zolumikizana, mphamvu zomwe zingatuluke zitha kupereka patani yamphamvu ya moyo wa mbumba. Ndipo pomwe chiwerengero cha anthu otenga mbali chimakula, mbali ina yatsopano inaonjezeredwa ku cholinga chawo chenicheni. Anabwera kudzatumikira ngati zipata zomwe achinyamata, akulu ndi maanja onse kuchokera ku mbumba yayikulu adzabwera ndi kukumana ndi Chibvumbulutso cha Bahá’u’lláh. Zinayamba kuonekanso momwe kunalili kotheka kuganizira njira zomwe ntchito yomanga mbumba mu kalasita: kadera kakakulupo kokhala ndi chikhalidwe ndi machitidwe a ntchito zachitukuko ndi chuma zofanana, kunalili kotheka. Kuthekera kokonzekera mapulani apafupi pa kalasita kunayamba kupezeka, ndipo kuchokera mu mapulani otere, maplogalamu a kukula kwa Chipembedzo anadzuka, olongosoledwa kukhala zomwe zinatchulidwa pambuyo pake mapulani a zochitika-chitika za miyezi itatu. Mbali imodzi yofunikira kutambasula inaoneka poyambilira pomwe: kuyenda kwa anthu mu mndandanda wa maphunziro a insitichuti kumapereka mangolomera ku, ndipo kumapitilizidwa ndi, kusuntha kwa makalasita pa mndandanda wa chitukuko. Ubwenzi uwu olumikizana unathandiza abwenzi ponse-ponse kuona momwe mbali za kukula mmalo owazungulira ndi kukonza njira ya mphamvu zopitilira. Pomwe nthawi imapita, panaoneka phindi kuona zomwe zimachitika mu kalasita kuchokera ku mbali zonse ziwiri za malamulo atatu a kuphunzira—kutumikira ana, achinyamata achisodzera, achinyamata ndi akulu—komanso kumbali ya masayiko a zochitika-chitika zofunikira ku mlingo wa kukula. Kulowa pang’ono mu ntchito za gawo la zaka makumi awiri ndi zisanu, zambiri mwa zinthu zomwe zinaoneka pa ndondomeko ya kukula komwe tikuona lero kunayamba kukhadzikika bwino.

5. Pomwe ntchito za abwenzi zimakula, mfundo zosiyana-siyana, njira ndi kachitidwe kofunikira ku ndondomeko ya kukula kunayamba kuwumbika mu dongosolo la ntchito lomwe lidzasintha ndikulora mbali zina zatsopano kukonzedwa. Dongosolo ili linaoneka kuti ndi lofunika pofuna kutulutsa mphamvu zamtundu wina. Zinathandiza abwenzi kulunjikitsa mphamvu zawo munjira zimene, upangiri unaonetsa kuti, zinali zofunikira ku kukula kwa mbumba za nthanzi.

Koma dongosolo si njira. Poyang’anira mbali zosiyana-siyana za dongosolo powunikira uweniweni wa kalasita, dera, kapena, dera lowandikana, patani ya chochitika itha kupangidwa yomwe ingalunjike pa zimene dziko lonse lachiBaha’i limaphunzira pomwe likukhalanso yankho ku zofunikira za dera limenelo. Kutsutsana pakati pa zofunikira zokakamira ndi kupanda malire pa zomwe munthu akudzikonda kunapereka njira yomvetsetsa yabwino ya kachitidwe kosiyanasiyana komwe anthu atha kuthandizira ndondomeko imene, pamtima pake, inali yololera mbali zonse ndi imene ikupitilirabe kuyikonza pomwe upangiri ukuchuluka. Pasakhale kukayika kulikonse pa kupita patsogolo komwe kunaperekedwa pachiyambi cha dongosolo ili: zotsatira zoluzanitsa ndi kuyanjanitsa ntchito za dziko lonse la chiBahá’í ndi kusonkhedzera kupita patsogolo kwake kunali zotsatira zazikulu.

6. Pomwe Pulani ina imayamba pambuyo pokutha kwa ina ndipo kulumikizana ndi ntchito yomanga mbumba imaonekeratu yokhazikika, zofunikira pa mlingo wa chikhalidwe unayamba kuoneka. Mwachitsano, kufunikira kophunzitsa mibadwo yachichepere kunayamikiridwa kwambiri, monga momwe kunaonekeranso kuthekera kwa achinyamata achisodzera makamaka. Mizimu yothandizana ndi kuyendera pamodzi panjira yogawana, kukulitsa sayiko ya kuthandizana, inakhala patani yomwe kuyesetsa kolunjika pa kutulutsa maluso otumikira kunapezedwa. Ngakhale kuchezerana kwa abwenzi akati pawo ndi iwo amene anawazungulira zinasintha, pomwe kuzindikira kunakwezedwa kwa mphamvu ya kukambirana kwa tanthauzo kuyatsa ndikuthandizira zofooka zauzimu. Ndipo chapamwamba kwambiri, mbumba za chiBahá’í zinatenga njira yapamtunda yolumikizanirana. Mzimu ulionse ovomera masomphenya a Chipembedzo umatha kukhala wotenga mbali wamphamvu—ngakhale wopititsa patsogolo kapena woyendetsa—wa zochitika-chitika za maphunziro, mikumano yopembedzera ndi mbali zina za ntchito yomanga mbumba; kuchokera mu mizimu imeneyi, ambiri amavomera chikhulupliro chawo mwa Bahá’u’lláh. Ndiko kuti, ganizo la ndondomeko ya kulowa mwaunyinji inayamba yomwe inadalira pang’ono pa zolankhula ndi zoganizira ndi kwambiri pa upangiri wopezeka wa momwe chiwerengero chachikulu cha anthu chingapezere Chipembedzo, kuchidziwa, kudzifanizira okha ndi zolinga zake, kuchita nawo zochita-chita zake ndi zokambirana, ndipo nthawi zambiri kuchilandira icho. Indetu, pomwe ndondomeko ya institichuti imalimbitsidwa mu chigawo ndi chigawo, chiwerengero cha anthu omwe amatenga nawo gawo mu ntchito ya Pulani, kufalikira ngakhale kwa iwo omwe anangodziwa kumene za Chipembedzo, chinakula kwambiri. Koma izi sizinachitike pongofuna kuchulukitsa chiwerengero. Masomphenya a munthu payekha ndi kusinthika kwa anthu onse kooneka nthawi imodzi, kopezeka pa kuwerenga Liu la Mulungu ndi kuyamikira kwa kuthekera kwa munthu wina kukhala wotenga mbali atatu mu sewero lozama zauzimu, kunapereka kuzindikira kwa ntchito ya cholinga chimodzi.

7. Chimodzi mwa zinthu zopatsa chidwi ndi zolimbikitsa mu nyengo ya zaka makumi awiri ndi zisanu izi ndi kutumikira komwe achinyamata a chiBaha’i anapereka, omwe ndi chikhulupiliro ndi kulimba mtima kwakulu pakati pa zolepheretsa zambiri apeza malo awo oyenelera patsogolo pa kuyesetsa kwa mbumba. Monga aphunzitsi a Chipembedzo ndi asuli a achichepere, ngati aphunzitsi oyenda-yenda ndi mapayoniya akudera lowandikana nalo, ngati makodineta a kalasita ndi mamembala a nthambi za chiBaha’i, achinyamata amakontineti asanu adzuka ndi kutumikira madera awo ndi kudzipereka ndi kudzikhuthura. Kukhwima mu nzeru komwe awonetsa, pogwira ntchito yomwe kupita patsogolo kwa Pulani Yoyera kukudalira, ndi chiwonetsero cha mphamvu zauzimu zawo ndi kudzipereka kwawo poyang’anira bwino tsogolo la mtundu wa anthu. Pozindikira kukhwima mu nzeru kopitilira uku, taganiza kuti, nyengo yotsatira Rizwani iyi, pomwe zaka zimene wokhulupilira atha kuloledwa kutumikira pa zikhadzikitso zikhalabe 21, zaka zimene wokhulupilira angathe kuvota m’masankho a chiBaha’i zatsitsidwa kufika pa 18. Tilibe kukayika kulikonse kuti achinyamata achiBahá’í kulikonseko omwe ali pa msinkhu umenewu atitetezera pa chikhulupiliro chathu mu kuthekera kwawo kukwaniritsa “mosamala ndi mosaopa”

“udindo wopatulika” omwe m’Bahai ovota aliyense wayitanidwa.

8. Tikuzindikira kuti, mwachilengedwe, mauweni-weni a madera amasiyana kwambiri. Mbumba zamdziko zosiyana-siyana, ndi malo osiyana-siyana mu mbumba zimenezo, anayamba mndandanda uwu wa Mapulani panthawi zosiyana-siyana za chitukuko; kuyambira pamenepo, apitanso patsogolo pa mlingo wosiyana-siyana ndipo akwaniritsa milingo yosiyana-siyana ya kupita patsogolo. Ichi, mwa icho chokha, sichachilendo. Zakhala chomwechi kuti zochitika mmalo zimasiyana, monga momwe mlingo wa malandilidwe umapezekera kumeneko. Koma tikuonanso, funde lalikulu, pomwe kuthekera, kudzikhulupilira ndi upangiri wochuluka wa mbumba zambiri ukupitira patsogolo, mokwezedwa ndi chipambano cha mbumba zoyandikana nazo ndi zapatali. Monga mwachitsanzo, pomwe mizimu yomwe inadzuka ndi kutsegula dera latsopnao mu chaka cha 1996 sanasowe chilichonse pa kulimba mtima, chikhulupiliro ndi kudzipereka, lero amnzawo kulikonse akuphatikiza makhalidwe omwewa ndi kuzindikira, kuphunzira ndi maluso omwe akhala akusonkhanitsidwa mu zaka makumi awiri ndi zisanu za kuyesetsa kwa dziko lonse la chiBahá’í world kulongosola ndi kukonza ntchito ya kukulitsa ndi kulimbitsa.

9. Posayang’anira kuti dera layambira pati, Lapititsa patsogolo ndondomeko ya kukula pomwe yaphatikiza makhalidwe a chikhulupiliro, kupilira ndi kudzipereka ndi kukonzekera kuphunzira. Motsindika, nkhani yonyaditsa mu mndandanda uwu wa Mapulani ndi kuzindikira kofalikira kuti kuyesetsa kopita patsogolo kumayamba ndi khalidwe la kuphunzira. Kuphweka kwa mfundo iyi kukutsutsa kufunika kwa zotsatira zomwe zimachokera mu ichi. Sitikukayika kuti mu kalasita iliyonse, itapatsidwa nthawi, idzapita patsogolo pa mndandanda wa chitukuko; mbumba zomwe zapita patsogolo mofulumira, mogwirizana ndi izo zomwe uweni-weni ndi kuthekera kwake kunali kofanana, zaonetsa kuthekera kobweretsa umodzi wa kaganizidwe ndi kuphunzira kufunika kw ntchito yadongosolo. Ndipo anapanga choncho popanda kukayika kuchitapo kanthu.

10. Kudzipereka ku kuphunzira kumatanthauzanso kukhala okonzeka kulakwitsa-ndipo nthawi zina, inde, kulakwitsa kumabweretsa madandaulo. Mosadabwitsa, njira zatsopano ndi machitidwe a zinthu sizinakonzedwe bwino koyambirira Kamba kosowa upangiri; pa nthawi ina; kuthekera kwatsopano kumatayika pomwe dera linali lotangwanika ndi kutumikira lina. Kukhala ndi malingaliro abwino si chitsimikizo kuti kulakwitsa sikungachitike, ndipo kuphunzira pa kudutsa apo kumafunika kudzichepetsa ndi kudzipatula. Pomwe dera lakhala lochilimika kuonetsa kupilira ndi kuphunzira mu kulakwitsa kwake komwe sikulephera, kupita patsogolo sikunalepherekepo.

11. Pakati-kati mu mndandanda wa Mapulani, kukhudzika kwa mbumba mu moyo wa dera kunayamba kukhala mbali yoonetserapo chidwi chachikulu. Okhulupilira analimbikitsidwa kuganizira izi kumbali ziwiri za ntchito zolumikizana—ntchito ya chitukuko ndi kutenga gawo mu zochitika-chitika za dera zofalikira. Izi, indetu, zinali mbali zina za ntchito ya kukulitsa ndi kulimbitsa, osati zosokoneza: zinali mbali imodzi yochokera mu ntchito imodzi. Kuchuluka kwa chiwerengero cha otumikira komwe dera limadalirapo, kudabweretsa kukula kwa kuthekera kwake kubweretsa nzeru zopezeka mu Chibvumbulutso cha Bahá’u’lláh polimbana ndi mavuto a tsiku lalero. Ndipo mavuto a mtundu wa anthu mu nyengo imeneyi kunaonetsa kufunikira kwa mankhwala ake ochiza operekedwa ndi Mchiritsi Woyera. Zomwe zimatanthauza mu zonsezi chinali chiyambi cha chipembedzo chosiyana ndizomwe ndi zodziwika padziko lonse lapansi: chiyambi chomwe chinazindikira chipembedzo ngati mphamvu yothamangitsa chitukuko chopitilira. Zinali zodziwika kuti kusinthika kotere sichionekera mwadzidzi, mwa kufuna kwake— inali ntchito ya otsatira Bahá’u’lláh kugwira ntchito kuti kusinthikaku kuonekere. Ntchito yotere inafunika kugwiritsa ntchito ndondomeko yomweyo ya kuphunzira kwa dongosolo ku ntchito ya chitukuko ndi kutenga mbali mu ntchito zokhudza onse.

12. Poyang’anira zamu zaka makumi awiri ndi zisanu, kuthekera kogwira ntchito zachitukuko kwakwera kwambiri, kupangitsa kufalikira kofulumira kwa ntchito. Poyerekeza ndi 1996, pomwe ntchito za chitukuko zokwana 250 zinapitilira chaka ndi chaka, tsopano alipo 1,500, ndipo chiwerengero cha zikhadzikitso zoyambitsidwa ndi aBaha’i chakula kudutsa 160. Ntchito zachitukuko za m’madera zoposa 70,000 za kanthawi kochepa zikuchitika chaka chilichonse, kukwera ndi makumi asanu. Tikuyembekezera kukwera kwa chiwerengero cha ntchito zimenezi kuchokera ku mathandizo odzipereka ndi mangolomera omwe tsopano akuperekedwa ndi

Chikhadzikitso Chachikulu chachiBaha’i pa Chitukuko (Bahá’í International Development Organization). Pakali pano, kutenga mbali kwa aBahá’í mu ntchito za chitukuko zomwe panopa zafalikira ponse ponse kwapita patsogolo. Pambali pa miyayi yochuluka pomwe abwenzi akumapereka mbali ya chiBaha’i mu zokambirana zomwe zimachitika malo a ntchito kapena pochezerana, kutenga nawo mbali kwa dongosolo mu zokambiranazi kwapitanso patsogolo kwambiri. Tikuganizira ntchito zofalikira osati za Mbumba YachiBaha’i Yakunja yokha—imene munyengo imeneyi yawonjezera maofesi ku Afirika, Asia ndi Europe—komanso ntchito yogwiridwa bwino ndi chilumikizo chachikulu chama ofesi a zochitika kunja kwadziko la chiBaha’i (External Affairs), omwe gawo ili la ntchito linakhala lofunikira; kuonjezera, panali maphunziro ndi zosonkhera zooneka zoperekedwa ndi okhulupilira paokha-paokha ku mbali zina zapadera zonsezi zikupita ku chifotokozo chachikulu, kuthokoza ndi kuyamikira komwe atsogoleri oganiza ndi ena odziwika pamilingo yonse ya dera awonetsa mobwereza-bwereza kwa Chipembezo, otsatira ake ndi ntchito zawo.

13. Powunika zaka 25 zonse, tili ozizwa ndi kupita patsogolo kosiyana-siyana komwe dziko lachiBaha’i lakwaniritsa pakamodzi. Moyo wake wa maphunziro wapiti patsogolo, osati pongotengera ntchito zake zomwe zakambidwa kale, komanso kuchuluka kwa zolemba-lemba zosindikizidwa ndi olemba za chiBaha’i, kupita patsogolo kwa mipata yofufuza mbali zina zokhudzana ndi chiphunzitso, ndinso kutukuka kwa seminale za maphunziro a chitukuko operekedwa ndi Insitichuti ya Maphunziro a Chitukuko cha Dziko lonse kwa achinyamata a msukulu zaukachenjede omwe anamaliza ndinso omwe akuphunzirabe , omwe, mogwirizana ndi zikhadzikitso za Chipembedzo, tsopano akutumikira achinyamata ochokera mmaiko osachepera 100. Kuyesetsa kamanga Nyumba Zopembedzeramo kwapitanso patsogolo kwambiri. Nyumba yomaliza Yopembedzeramo inamangidwa ku Santiago, Chile, ndi pulani yofuna kumanga nyumba ziwiri za m’dziko zotumikiramo ndi zina zisanu m’madera inayambika; Nyumba Yopembedzeramo ku Battambang, Cambodia, ndi Norte del Cauca, Colombia, zatsegulidwa kale. Nyumba Zopembedzeramo, kaya zatsopano kapena zakale, zikupitilira kutenga mtima wa moyo wa mbumba. Thandizo la katundu operekedwa ndi okhulupilira ku ntchito zochuluka zomwe abwenzi a Mulungu akugwira lakhala lochuluka. Ngati ntchito yapafupi yapamodzi ya kutukuka kwa uzimu. Kudzipereka ndi kudzikhuthura komwe, panthawi ya msautso wa zachuma, kusonkhera kuthumba kwakhala kopitilira –indedi, kolimbitsidwa- mosaneneka. Mu khalidwe la kayendetsedwe ka chiBaha’i, kuthekera kwa Mabungwe Auzimu Aakulu kukwaniritsa zofuna za mbumba zawo ku mbali zonse kwapititsidwa patsogolo. Apindula mwapadera kumbali ziwiri zapamwamba za kugwilira ntchito limodzi ndi maKhansala, ameme akhalanso zida zodalilika mobweretsa dongosolo la kutolera zophunziridwa kuchokera ku madera padziko lonse ndi kuonetsetsa kuti zikugawidwa ponse ponse. Iyinso inali nyengo momwe Makhonsolo a Mzigawo anatuluka kukhala zikhadzikitso zodziyimira pazokha za Chipembedzo, ndipo zikupezeka mzigawo zokwana 230 tsopano, makhonsolo ndi ma insitichuti ophunzitsa omwe akuyang’anira zaonetsa zokha kuti ndi zofunikira popititsa patsogolo ndondomeko ya kukula. Pofuna kutambasulira mtsogolo ntchito za Wamkulu Woyang’anira Ḥuqúqu’lláh, Dzanja la Chipembedzo cha Mulungu ‘Alí-Muḥammad Varqá, Bodi yayikulu ya Woyang’anira Ḥuqúqu’lláh inakhadzikitsidwa mu chaka cha 2005; lero ikulumikizitsa kuyesetsa kwa woyang’anira a mzigawo zosachepera 33 ama Bodi a mmaiko ndinso mzigawo padziko lonse, omwe mmalo mwake akutsogolera ntchito ya Woyimira opitilira 1,000. Zitukuko zomwe zinachitika ku Malo Oyera mu nyengo imeneyi ndi zambiri: tinachitira umboni kumalizitsa kwa masitepe (Terraces) a Malo Owusirako a Báb ndi nyumba ziwiri ndi kuyambika kamanga Nyumba Yowusiramo ya

‘Abdu’lBahá, osayiwala ntchito zina zolimbitsa ndi kuteteza Malo Oyera a Chipembedzo. Malo Owusira a Bahá’u’lláh Báb anazindikiridwa ngati amodzi mwa malo ozizwitsa (World Heritage) padziko lonse, malo a mtengo wapatali ku mtundu wa anthu. Anthu amathamangira ku malo opatulikawa mu unyinji wawo, kufika pafupi-fupi theka la miliyoni zaka zina, ndi Sentala ya Dziko lonse imalandira alendo mazana pakamodzi, nthawi zina kudutsa 5,000 m’chaka chimodzi, kuphatikizapo alendo achiBahá’í; ndife wokondwa pa chiwerengero chochuluka monga momwenso tilili okondwa ndi ndi mitundu ya anthu osiyana-siyana ndi maiko omwe amayimira pakati pa iwo amene amabwera ku ulendo woyera (pilgrimage). Kumasulira, kusindikiza ndi kutumiza mbali zonse kwa Malembo Woyera kwapitanso patsogolo, pamodzi ndi kupititsa patsogolo kwa Nkhokwe ya Malembo a chiBaha’i (Bahá’í Reference Library), imodzi mwa nkhokwe zapa intaneti zolumikizana ndi Bahai.org, yomwe mwa iyo yokha tsopano ikupezeka mu ziyankhulo zokwana khumi. Mitundu ya maofesi yosiyana-siyana ndi nthambi zina zakhadzikitsidwa, ku Malo Oyera ndinso madera ena, zothandizira ndondomeko ya kuphunzira komwe kukutambasuka mbali zosiyana-siyana za ntchito mdziko lonse la chiBaha’i. zonsezi, abale andi alongo athu mu chikhulupiliro, ndipang’ono chabe mwa nkhani zomwe tingakambeko za zomwe kudzipereka kwanu kwa Iye Amene anali Wolakwiridwa wa Dziko Lapansi anabweretsa.

Titha kungobwerezako mawu oswetsa mtima omwe ananenapo Abdu’l-Baha pamene, atakhudzika kwakukulu analira mokweza: “O Bahá’u’lláh! Mwachitanji?”

14. Pamwamba pa kota ya zaka zana limodzi, tsopano tionetsetse pa Pulani ya Zaka Zisanu yomwe yangothayi, Pulani yosafanirizika ndi ina iliyonse munjira zosiyana-siyana. Mu Pulani iyi tidamema aBaha’i a dziko lapansi kuti atute zonse zomwe adaphunzira mu zaka makumi awiri zapita ndi kuzigwiritsa ntchito mokwanira. Ndife okondwa kuti ziyembekezo kumbali iyi zinadutsa mlingo wokwaniritsidwa, komabe pomwe mwachidziwikire tikuyembekeza zinthu zazikulu kuchokera kwa Otsatira a Wokongola Wodalitsikayo, maonekedwe a zomwe zinakwaniritsidwa kudzera mu kugwira ntchito modzikhuthura kunali kotenga mtima. Inali Tsonga la chimake cha chikwanilitso cha zaka 25.

15. Pulani inali yapadera ndi chikumbukiro cha zikondwelero zoyera ziwiri, chilichonse mwa izi chinabweretsa moto wapadera ku mbumba padziko lonse. Gulu la wokhulupirika linaonetsa, pa mlingo omwe sunaonekenso ndi mosavuta, kuthekera kokhudza anthu a mbali zonse polemekeza moyo wa m’Bvumbulutsi wa Mulungu. Chinali chizindikiro cha chinthu chinachake chachikulu: kuthekera kobweretsa pamodzi kutuluka kwa mphamvu zauzimu pa kupita patsogolo pa Chipembedzo. Kulandiridwa kwake kunali kopambana mwakuti mmadera ambiri Chipembedzo chinadziwika pamlingo wadziko. Mmalo ena momwe sizinayembekezeke, kapena kusang’anirapo, kulandira kwa anthu kwa Chipembedzo kunali koonekeratu. Mazana ndi mazana ndi mazana a anthu anatengedwa ndi kukumana kwa mzimu wa pemphero omwe lero ndi chizindikiro cha mbumba zachiBaha’i kulikonse. Masomphenya a chomwe chimapangidwa kutheka posangalalira Tsiku Loyera la chiBaha’i anakulitsidwa kwambiri.

16. Chipambano cha Pulani, mu nambala zomveka bwino, chinadutsa mofulumira awo onse a Mapulani a kumbuyo chiyambireni 1996. Pomwe Pulani iyi imayamba, panali kuthekera kopanga zochitika-chitika zopitilira 100,000 panthawi, kuthekera komwe kunali chipatso cha zaka 20 za ntchito yapamodzi. Tsopano zochitika-chitika zoposa 300,000 zikuchitika. Kutenga mbali mu zochitika-chitika zimenezi kwadutsa pa mamiliyoni awiri, kukwera patatu. Pali zikhadzikitso za insitichuti mmako ndi mzigawo zokwana 329 zomwe zikugwira ntchito, ndipo kuthekera kwawo kukuonekera mu umboni wakuti tsopano anthu okwana mazana 750 akwaniritsa kumalizitsa buku limodzi pa mndandanda wa mabuku a insitichuti; onse pamodzi, chiwerengero cha makozi omwe amalizidwa ndi anthu tsopano chili mamiliyoni awiri kukwera pafupi-fupi ndi theka ndi kota mu zaka zisanu.

17. Kukula kwa kutsindika komwe mapologalamu a kukula a kathithi akuchitidwira kukufotokoza nkhani yosangalatsa paokha. Mu zaka zisanu izi, tidapempha kuti kukula kwa kathithi kufalikire mu makalasita okwana 5,000 omwe kudayamba kale. Chitsogozo ichi chidakhala mangolomera ogwira ntchito modzipereka padziko lonse. Zotsatira zake, chiwerengero cha makalasita omwe ali ndi pologalamu ya kukula mwakathithi chidawonjezereka kwakulu tsopano chili pafup-fupi 4,000. Zovuta zomwe zinapezeka potsegula midzi ndi madera owandikana atsopano ku Chipembedzo mkatikati mwa chipwilikiti cha matenda padziko lonse, kapena kukulitsa zochitika-chitika zomwe zinali zosakhazikika pomwe mliri umayambika, zinalepheretsa kuti chiwerengero chachikulu chikwaniritsidwe mu chaka chomaliza cha Pulani. Komabe, pali zambiri zoti zikambidwe kuposa izi. Poyambilira pa Pulani, tidafotokoza chiyembekezo kuti chiwerengero cha makalasita komwe abwenzi anadutsa mtunda wachitatu (IPG) pa mndandanda wa kukula, ngati chotsatira chophunzira momwe angalandilire chiwerengero chochuluka mu zochitika-chitika zawo, chidzakula ndi mazana owonjezera. Chiwerengero chimenechi nthawi imeneyo chinali pa 200, m’maiko pafupi-fupi. Zaka zisanu zadutsapo, chiwerengero ichi Chakwera kufika pa 1,000 m’maiko pafupi-fupi 100—kota ya mapologalamu onse a kukula mwakathithi m’dziko lonse, chikwaniritso chomwe chadutsa chiyembekezo chathu. Koma ngakahle chiwerengero ichi sichikuwulura utali omwe mbumba zafikirapo. Pali makalasita oposa

30 komwe chiwerengero cha zochitika-chitika zomwe zikupita patsogolo zikudutsa 1000; m’malo, chiwerengero chonse chikukwana mazana-mazana, kuphatikiza kutenga mbali kwa anthu opitilira 20,000 mu kalasita. Chiwerengero chokwera cha Mabungwe Auzimu Aang’ono tsopano akuona kutambasuka kwa mapologalam a maphunziro omwe akutumikira kwa ana onse ndi achinyamata achisodzera; izinso zayamba kuoneka m’madera ena a mmizinda. Kukumana ndi Chibvumbulutso cha Bahá’u’lláh, kwapangitsa, pa zitsanzo zooneka, kukweza anthu, maanja ndi abale ena— zomwe zikuoneka mu kuyenda kwa unyinji kulunjika ku cholinga chapamodzi. Nthawi zina, kusamvana kwakale-kale pakati pa magulu awiri otsutsana kukusiyidwa pambuyo, ndipo ntchito zina za dera ndi mphamvu zina zikusinthika potsatira kuwala kwa ziphunzitso zoyera.

18. Sitingakhale osakondwa pa zinthu zonyaditsazi. Mphamvu zomanga dera za Chipembedzo cha Bahá’u’lláh zikutulutsidwa ndi kutambasuka kwakukulu, ndipo awa ndi maziko olimba pomwe Pulani ya Zaka Zisanu ndi Zinayi ikubwerayi idzamangidwapo. Makalasita a mphamvu zodziwika, monga momwe kunayembekezeredwa, akhala nkhokwe za kuphunzira ndi mathandizo kwa owandikana nawo. Ndipo zigawo komwe makalasita oterewa adutsa imodzi apititsa patsogolo mosavuta njira zothamangitsira kukula mu kalasita ndi kalasita. Tili okakamizidwa kutsindika kawiri, komabe, kuti kupita chitsogolo kwafalikira, kusiyana pa kupita patsogolo pakati pa malo amodzi ndi ena ndikwa muyeso. Kumvetsetsa kwapamodzi kwa mbumba pa ndondomeko ya kulowa mwaunyinji ndi kudzikhulupilira kwake pokwaniritsa kulimbikitsa ndondomeko imeneyi mu nyengo zina zilizonse kwakwera kufika pa mlingo omwe sunaganiziridwe ndikale lonse. Mafunso ozama omwe anakhala akutuluka kwa nthawi yayitali, ndi omwe anayikidwa mu chindunji mu chaka cha 1996, akhala akuyankhidwa mokhutira bwino ndi dziko la chiBaha’i. pali m’badwo wa okhulupilira omwe miyoyo yawo yonse akhala akuchitira umboni kupita patsogolo kwa mbumba. Koma mlingo waukulu wa zimene zachitika mmakalasita ochulukawa komwe danga la kuphunzira lakhadzikitsidwa lakulitsa kwambiri ndondomeko ya kulowa mwaunyinji kukhala yofunikira ya magawo a mbiri.

19. Ambiri akukumbukira momwe Mtchinjilizi anagawira Ndime za Chipembedzo mu magawo otsatana; gawo loyamba ya Ndime Yomanga linayamba chaka cha 2001. Zomwe zikudziwika pang’ono ndi zoti Mtchinjilizi anapereka umboni kuti kuli magawo a Pulani Yoyera, ndi ndime mkati mwa magawo amenewo. Zinayimitsa kwa zaka makumi aiwiri pomwe zikhadzikitso za mmadera ndi mmaiko za Ndondomeko ya Kayendetsedwe zimakhadzikitsidwa ndi kulimbitsidwa, Pulani Yoyera yokonzedwa ndi ‘Abdu’l-Bahá inakhadzikitsidwa mu chaka cha 1937 ndi kuyambika kwa ndime yoyamba ya gawo loyamba: Pulani ya Zaka Zisanu ndi Ziwiri (7) yokhadzikitsidwa ndi Mtchinhilizi ku mbumba ya chiBaha’i yakumpoto kwa Amerika. Gawo loyamba linatsekedwa kumapeto a Zaka Khumi za Kampeni muchaka cha 1963, yomwe zotsatira zake zinali kudzalidwa kwa mbendera ya Chipembedzo padziko lonse. Ndime yotsegulira ya gawo lachiwiri ina Zaka Zisanu ndi Zinayi (9) zoyambilira, ndipo ma Pulani osachepera khumi anatsatira, Mapulani omwe anali a zaka zapakati pa chimodzi ndi zisanu ndi ziwiri (7). Poyambilira pa gawo ili lachiwiri, dziko la chiBaha’i linali litaona kale chiyambi cha kulowa mu Chipembedzo mwaunyinji komwe Mlembi wa Pulani Yoyera analosera kale; mu zaka zotsatira, mibadwo ya okhulupilira odzipereka mu mbumba ya Dzina Lalikulu Koposa agwira ntchito mu Munda Woyera kubzala zoyenelera kubweretsa kukula kwakukulu kopitilira. Ndipo pa nyengo ino yaulemelero ya Rizwani, zipatso zimenezi ndi zochuluka bwanji! Kuonekera kwa chiwerengero chabwino chomwe chikutenga mbali mu zochita-chita za mbumba, kugwira kuwala kwa chikhulupiliro ndi kudzuka ndi kutumikira mofulumira kumayambiliro a Pulani yachoka pa chidwi chobwera ndi chikhulupiliro ndipo tsopano ndi choonadi chobwerezabwereza. Kupita patsogolo koonekeratu ndi kolozeka uku kukufuna kuzindikiridwe mu mabuku a Chipembedzo. Ndi mitima yosangalala, tikulengeza kuti gawo lachitatu la Pulani Yoyera ya Mtchinjilizi yayamba. Ndime ndi ndime, gawo ndi gawo Pulani yake imasulidwa, mpaka kuwala kwa Ufumu kuwalitse mtima ulionse.

20. Abwenzi okondedwa, kuunikira kwa ntchito ya zaka zisanu yomwe yamalizitsa ndime yachiwiri ya Pulani Yoyera kukhala kosakwanira popanda kutchulapo zovuta zomwe zinaperekeza mu chaka chomaliza zomwe zikupitilira mpaka pano. Kuletsa kuchitira zinthu pamodzi kwa anthu komwe kunakula ndi kuchepa mmaiko ambiri mu nyengo imeneyi kukanatha kugwetsa kuyesetsa kwa pamodzi kwa mbumba, komwe kuchira kwake kukadatenga zaka, koma pali zifukwa ziwiri zomwe izi sizidakhalire chomwecho. Choyamba kunali kukhudzika kofalikira kwa udindo wa aBaha’i kutumikira mtundu wa anthu, mochuluka kuposa mu nthawi ya masautso ndi mavuto. Chawiri chinali kudzuka kodabwitsa mu kuthekera kwa dziko la chiBahá’í poyankhapo pa kukhudzika kumeneku. Chizolowezi cha zaka zambiri chophunzira patani ya kugwira ntchito mwa ndondomeko, abwenzi anabweretsa maluso awo ndi ganizo la cholinga kukwaniritsa kunyamula chionongeko chosakonzekereka, kwinaku akuonetsetsa kuti njira zatsopnao zomwe akugwiritsa ntchito zinali zogwirizana ndi ndondomeko zomwe anayesetsa mu ma Pulani akumbuyo kudzisula kuti zikhale zangwiro. Ichi sikufuna kupepusa zovuta zazikulu zomwe aBaha’i akukumana nazo, monga akuchitira amnzawo padziko lonse; komabe mu nyengo ya zovuta zawo yonse, okhulupilira akhala oima njii. Mathandizo aperekedwa ku mbumba zomwe zimafuna thandizo, masankho anachitika komwe kunali kuthekera, ndipo mu nyengo zonse zikhadzikitso za Chipembedzo zapitilira kugwira ntchito zawo. Pakali pena kutenga ndime zikulu-kulu popita chitsogolo. Bungwe Lauzimu Lalikulu la São Tomé ndi Príncipe likhadzikitsidwanso mu nyengo iyi ya Rizwani, ndipo nsanamira zina ziwiri ya Nyumba ya Chilungamo ya Amitundu zidzutsidwa: Bungwe Lauzimu Lalikulu la Croatia, ndi likulu la ku Zagreb, ndi Bungwe Lauzimu Lalikulu la Timor-Leste, ndi likulu lake ku Dili.

21. Tsopano Pulani ya Chaka Chimodzi yayamba. Cholinga ndi zofunikira zake zinafotokozedwa kale mu uthenga wathu womwe unatumizidwa pa Tsiku la Pangano; Pulani iyi, ngakhale yayifupi, ikwaniritsa kukonzekeretsa dziko la chiBahá’í ku Pulani ya Zaka 9 yomwe itsatire. Nyengo ya mphamvu zapadera, yomwe inatsegula zaka 100 pomwe ma Tabuleti a Pulani Yoyera anavumbulutsidwa, itsekedwa posachedwa ndi zaka 100 zakukwera kumwamba kwa ‘Abdu’l-Bahá, kukwaniritsa mathero a zana loyamba la Nyengo Yomanga (Formative Age) ndi kuyambika kwa yachiwiri. Gulu la wokhulupirika likulowa Pulani iyi yatsopano panthawi yomwe mtundu wa anthu, modzichepetsa ndi kufooka kwake ukuoneka kuti ukuzindikira kufunika kogwirana manja pothana ndi mavuto a dziko lonse. Komabe, zizolowezi zopikisana, kudzikonda, tsankho ndi kusamasukirana zikupitilira kusokoneza ulendo wa umodzi, ngakhale chiwerengero chachikulu cha anthu omwe akuonetsa mu mau komanso ntchito momwe iwonso, akufunitsitsa kuvomereza kwakulu kwa umodzi wa anthu wamkati. Tipemphera kuti maanja a dziko lapansi akwaniritse kuyika pambali kusiyana kwawo pofuna kupititsa patsogolo zabwino. Posayang’anira zotchinga zomwe zakutira miyezi ikubwerayi, tikupempha Bahá’u’lláh kulimbitsa chikhulupiliro chomwe chalimbikitsa omtsatira Ake kwa nthawi yayitali kuti chichuluke kuti, mupite patsogolo mu ntchito yanu, kuchilimika kwanu kusasokonezedwe ndi mafunde a dziko amene kufunitsitsa kwakukulu kwa uthenga wochiritsa kuli koonekeratu.

Pulani Yoyera ikulowa nyengo yatsopano ndi ndime yatsopano. Tsamba latsekulidwa.

 

Windows / Mac