Return to BahaiPrayers.net   Facebook

Amene akufuna kupempherayo, asambe manja ake, ndipo pamene ali kusamba, anene kuti:

Limbikitsani dzanja langa. O Mulungu wanga, kuti ligwire Bukhu Lanu ndi chilimbiko chomwe makamu a dziko lapansi sadzakhala ndi mphamvu kuligonjetsa. Litchinjirizeni tsono, kuti lisadudukire mchilichonse chomwe sichailo. Ndithudi, Inu muli Wanyonga, Wamphamvu Zopambana.

Ndipo pamene akusukusula nkhope yake iye anene kuti:

Ndatembenukira nkhope yanga kwa Inu, O Ambuye wanga! Iwalitseni ndi kuunika kwa nkhope Yanu. Itetezeni, chomwecho, posatembenukira kwa wina koma

Inu.

Tsopano ayimilire ndipo ayang’ane ku Qiblih (ku Bahji, Akka), iye anene kuti:

Mulungu achitira umboni kuti kulibe Mulungu wina koma Iye. Maufumu a Chibumbulutso ndi chilengedwe ndi Ake. Iye, muchoonadi, wabvumbulutsa Iye Amene adayankhula pa Sinai, amene kubzolera mwa Iye Dangaliro lopambana lawalitsidwa, ndipo Mtengo wa Loti umene paseri pake palibe podzera wayankhula, ndipo kubzolera mwa Iye chiitano chalengezedwa kwa onse amene ali m’mwamba ndi padziko lapansi: “Taonani Mwinizonse wabwera. Dziko lapansi ndi kumwamba, ulemelero ndi ulamuliro ndi wa Mulungu, Ambuye wa anthu onse, ndi Mwini wa za m’mwambamo ndi pansi pano!”

Tsopano Iye, aweramira pansi, manja ali pa maondo ndi kunena kuti:

Wokwezeka Ndinu pamwamba pa chitamando changa ndi chitamado cha wina aliyense pambali panga, opitirira chifotokozo changa ndi chifotokozo cha onse amene ali kumwamba ndi onse amene ali pa dziko lapansi!

Tsopano iye ayimirire atatambasula manja ake zikato zitapenya kumwamba molunjika nkhope, ndi kunena kuti:

Musamukhumudwitse, O Mulungu wanga, Iye amene, ndi zala zodandaula, wakakamira ku mpindiro wa chifundo Chanu ndi chisomo Chanu, O Inu Amene mwa iwo amene alangiza Chifundo Chopambana!

Ndipo iye akhazikike pansi, ndi kunena kuti:

Ndichitira umboni ku umodzi Wanu ndi chiphatikizo Chanu, ndi kuti Inu Mulungu, ndipo kuti kulibenso Mulungu wina pambali Panu, Inu, ndithudi, mwaulula Chipembedzo Chanu, mwakwaniritsa Pangano Lanu, ndi kutsegulitsa chitseko cha chisomo Chanu kwa onse amene akhala kumwamba ndi dziko lapansi. Dalitso la mtendere, malonje ndi ulemelero, zikhale pa okondedwa Anu, amene zosintha ndiponso mwayi wa dziko lapansi sizidawalepheretse kutembenukira kwa Inu, ndipo amene adapereka zawo zonse, m’chiyembekezo chokapeza chijacho chimene chilli ndi Inu. Inu zedi, muli Wokhululukira-khululukirabe, Wachaulere Chonse.

(Ndipo ngati wina aliyense atasankha m’malo mwa ndime yayitali atangonena mawu awa: “Mulungu achitira umboni kuti kulibe Mulungu wina koma Iye, Wothandiza Patsoka, Wodzidalira Yekha,” ndipokwanira. Chimodzimodzi ndipokwaniranso ngati iyeyo atakhazikika pansi asankhe kunena mawu awa: “Ndichitira umboni ku umodzi Wanu ndi chiphatikizo Chanu, ndipo kuti Inu Ndinu Mulungu, ndi kuti kulibe

Mulungu wina pambali Panu.”)

 


English  
ភាសាខ្មែរ  
አማርኛ.  
Afrikaans  
Alaska Native  
American Indian  
Azərbaycan  
Bahasa Indonesia  
Bahasa Malaysia  
Bidayuh  
Bosanski  
Canadian Indigenous  
Català  
Cebuano  
Česky  
Chamorro  
Chichewa  
Corsica  
Cymraeg  
Daga  
Dansk  
Deutsch  
Dzongkha  
Eesti  
Español  
Esperanto  
Euskara  
Fiji  
Filipino  
Føroyar  
Français  
Frysk  
Hausa  
Hawaiian  
Hiri Motu  
Hrvatski  
Irish  
Íslenska  
Italiano  
Kabyle  
Kalaallisut  
Kiribati  
Kiswahili  
Kreyol Ayisyen  
Kuanua  
Kube  
Latviešu  
Lëtzebuergesch  
Lietuvių  
Luganda  
Magyar  
Malagasy  
Malti  
Māori  
Marshallese  
Melpa  
Montenegrin  
Nalik  
Namibia  
Nederlands  
Norsk  
Papiamentu  
Polski  
Português (BR)  
România  
Sámi  
Samoan  
Sarawak  
Sesotho  
Shqip  
Slovenščina  
Slovensky  
Sranan Tongo  
Srpski српски  
Suomi  
Svenska  
Tetum  
Tiếng Việt  
Tok Pisin  
Tongan  
Türkçe  
Türkmençe  
Tuvalu  
Vanuatu  
ελληνικά  
Беларускі  
български  
Кыргыз  
Монгол хэл  
Русский  
Тоҷикӣ  
Україна  
հայերեն  
اُردُو  
العربية  
فارسی  
नेपाली  
मराठी  
हिंदी  
বাংলা  
ગુજરાતી  
ଓଡ଼ିଆ  
தமிழ்  
తెలుగు  
ಕನ್ನಡ  
മലയാളം  
ภาษาไทย  
ພາສາລາວ  
한국어  
日本語  
简体中文  
繁體中文  
Windows / Mac