Return to BahaiPrayers.net
Facebook
O Mulungu wanga, Mbuye wanga, mathero Achofuna changa, uyu, wantchito Wanu, afuna kugona mum’thunzi wa chifundo Chanu, ndikupumula pansi pa chifungatira cha chisomo Chanu, akupempha chisamaliro Chanu ndi chitetezo Chanu.
Ine ndikupemphani Inu, O Ambuye wanga, kuti ndi diso Lanu limene siligona, mulonde maso anga kuti asayang’ane china pambali pa Inu. Limbikitsani, choncho masomphenya ake kuti aone zizindikiro Zanu, ndikuyang’ana ku mzere wa Chibvumbulutso Chanu. Inu ndinu amene patsogolo pa zibvumbulutso za ukulu Wanu, maonekedwe amphamvu agwedezeka.
Kulibe Mulungu wina koma Inu, Wamphamvu Zonse, Wogonjetsa Onse, Wosakakamizidwa.
- Bahá'u'lláh