Return to BahaiPrayers.net
Facebook
O ofufuza Choonadi! Ngati ukukhumba kuti Mulungu atsegule maso ako, uyenera kupempha kwa Mulungu, kupemphera ndi kuyankhula Naye pakati pausiku, ndi kunena:
O Ambuye, Ndatembenuzira nkhope yanga ku ufumu
Wanu wa umodzi ndi kudzimiza m’nyanja ya chifundo Chanu. O Ambuye, walitsani maso anga powona kuwala Kwanu pakati pa usiku uno, ndi kundipanga kukhala osangalala ndi vinyo wa chikondi Chanu mu m’badwo wopambanawu. O Ambuye, ndipangeni kuti ndimve kuitana Kwanu, ndipo tsengulani pamaso anga zitseko zakumwamba Kwanu, choncho kuti ndiwone kuwala kwa ulemerero Wanu ndi kukopedwa ndi kukongola Kwanu.
Indetu, Inu ndi Wopatsa, Woolowamanja, Wachifundo, Wokhululukira.
- `Abdu'l-Bahá