Return to BahaiPrayers.net
Facebook
O Mulungu! Lelani kakhanda aka pa chifungatiro chachikondi Chanu, ndipo mukapatse mkaka wochokera kumaere a Mphatso Yanu. Samalirani kachomeraka m’munda wamaluwa wa chikondi Chanu ndikukathandiza kukula kubzolera mumbvumbi wa chaulere Chanu. Kapangeni kukhala kamwana ka Ufumu ndipo katsogozeni kumwamba Kwanu. Inu Ndinu wamphamvu ndi wokoma mtima, ndipo Inu Ndinu Wopatsa, Wosamana, Ambuye a chaulere chopambana.
- `Abdu'l-Bahá