Return to BahaiPrayers.net
Facebook
O Inu a Chifundo Ambuye! Ndine mwana wamng’ono, ndikwezeni ine pondilora ine ku ufumu. Ndili wa dziko lapansi, ndipangeni ndikhale wakumwamba, ine ndili wotsika padziko, ndiloleni ine ndikhale wa maiko am’mwamba; mdima, ndifuteni ine kuti ndikhale woyera; chinthu cha dziko ndipangeni ine wauzimu, ndipo ndipatseni kuti ndi bvumbulutse mphatso Zanu zopanda malire. Inu ndinu Wamphamvu, Wachikondi Chonse.
- Bahá'u'lláh