Return to BahaiPrayers.net
Facebook
O Ambuye anga! O Ambuye anga! Ine ndine mwana wa zaka zochepa. Ndidyetseni ine kuchokera ku mawere a chifundo Chanu, ndipangeni ine kukhala muchifungatiro chachikondi Chanu, ndiphunzitseni ine musukulu ya chitsogozo Chanu ndipo mundipambanitse ine pansi pa nthunzi wa mphatso Yanu. Ndilanditseni ine kuchokera mu mdima, ndipangeni ine kukhala kuwala konyezimira; ndichotsereni ine kusakondwa, ndipangeni ine kukhala duwa m’munda wa lozesi, ndiwalitseni ine kukhala wantchito pakhomo Lanu loyera ndipo perekani kwa ine makhalidwe a umunthu ndi chilengedwe cha chiyero; ndipangeni ine chiyambi cha mphatso kwa wanthu adziko lapansi ndipo vekani mutu wanga ndi chisoti cha moyo wosatha. Indetu, Inu ndinu Wamphamvu, Wamkulu, Woona, Wakumva.”
- `Abdu'l-Bahá