Return to BahaiPrayers.net
Facebook
Pamene mulowa mchipinda chokumanira, nenani pemphero ili ndi mtima wogunda ndi chikondi cha Mulungu ndi lirime loyeretsedwa kuzonse koma chikumbukiro Chake, kuti Wamphamvu Zonseyo mwachifundo Akuthandizeni kupeza chipambano chachikulu:
O Mulungu, Mulungu wanga! Ife tili antchito Anu amene tatembenukira modzipereka kunkhope Yanu yoyera, amene tadzilekanitsa tokha kuzinthu zonse kupatula Inu pa Tsiku loyera-yerali. Ife tasonkhana mu
Bungwe la Uzimu ili, wogwirizana m’malingaliro athu ndi m’maganizo athu, ndi mzolinga zathu zobvomerezana kukweza Mau Anu pakati pa anthu. O Ambuye, Mulungu wathu! Tipangeni ife kukhala zizindikiro za Chitsogozo Chanu choyera, mbendera za Chikhulupiliro Chanu chokwezeka pakati pa anthu, antchito kuchipangano
Chanu champhamvu, O Inu Ambuye wathu wam’mwambamwamba, abvumbulutsi a umodzi Wanu Woyera mu ufumu Wanu wa Abha, ndi nyenyezi zowala zowunikira maiko onse.
Ambuye! Tithandizeni ife kuti tikhale nyanja zoyendetsedwa ndi mafunde a chisomo Chanu chodabwitsa, mitsinje yoyenda kuchokera kumitundu Yanu yoyera-yera, zipatso zabwino pa mtengo wa chiphunzitso Chanu cha kumwamba, mitengo yogwedezedwa ndi mphepo ya Chaulere Chanu m’munda Wanu wakumwamba. O Mulungu! Pangani mizimu yathu kutsamira pa malemba a Umodzi Wanu woyera, mitima yathu kukondweretsedwa ndi m’bvumbi wa chisomo Chanu, kuti tigwirizane ngati mafunde a m’nyanja imodzi ndikulumikizana ngati Malawi akuwala Kwanu kwakukulu; kuti maganizo athu, malingaliro athu, kumva kwathu kukhale ngati choona chimodzi, kusonyeza mzimu wa umodzi kubzolera mdziko lonse lapansi. Ndinu wa Chisomo, wa Chaulere, Wopatsa, wa Mphamvu Zonse, wa Chifundo, Wachisoni.
- `Abdu'l-Bahá