Return to BahaiPrayers.net
Facebook
Dzina Lanu ndilo kuchira kwanga, O Mulungu wanga, ndipo kukumbukira Inu ndi mankhwala anga. Kuyandikira kwa Inu ndi chiyembekezo changa, ndipo kukonda Inu ndibwenzi langa. Chifundo Chanu kwa ine ndikuchitira kwanga ndi chithandizo changa m’dziko lino ndi mdziko liri nkudza. Inu, ndithudi, Ndinu wa chaulere chonse, Wodziwa Zonse, Wanzeru Zonse.
- Bahá'u'lláh