Return to BahaiPrayers.net
Facebook
Ulemerero ukhale kwa Inu, O Mbuye Mulungu wanga! Ndikupemphani Inu m'dzina Lanu. kupyolera mmene Iye Amene Ndiye kukongola Kwanu, wakhazikitsidwa pa ufumu wa Chipembedzo Chanu, ndipo ndi m'dzina Lanu kupyolera m'lomwero musintha zinthu zonse ndipo musonkhanitsa zinthu zonse pamodzi, ndi kuitana zinthu zonse ku bwalo ndikusupa zinthu zonse, ndi kuteteza zinthu zonse. Ndikupemphani Inu kulondera mdzakaziyu amene wathawira ku mpumulo Wanu ndipo wafunafuna mthunzi wa Amene mwa Iye Inu mwaonekeramo ndipo waika chikhulupiriro ndi chigomezero chake chonse mwa Inu.
Mdzakaziyu akudwala, O Mulungu wanga ndipo walowa kunsi kwa mthunzi wa Mtengo wa machiritso Anu, wokanthidwa, ndipo wathawira ku Mzinda wa chitetezo Chanu, wadwala, ndipo wafunafuna Mutu wa Kasupe wa kukoma mtima Kwanu; wobuwula ndi ululu, ndipo wakangazira kuti akapeze Chitsime cha Mweza wa kudekha Kwanu; walemedwa ndi tchimo, ndipo walunjikitsa nkhope yake ku bwalo la chikhululukiro Chanu.
Muvekeni iye, mwa ulamuliro Wanu ndiponso mwa chikondi cha kukoma mtima Kwanu, O Mulungu wanga ndi Wokondedwa wanga, ndi chovala cha chitonthozo ndi kuchiritsa Kwanu, ndipo mpangeni iye kumwera mu chikho cha chifundo ndi kukoma mtima Kwanu.
Mtetezeni iye, makamaka ku zovuta ndi zopweteka zonse, ku zowawa zonse ndi matenda ndiponso kuchokera ku chiri chonse choyipa kwa Inu.
Inu, m'chowonadi, Muli Wokwezeka kopambana pamwamba pa zonse kupatula Inu Mwini. Inu indetu, Ndinu Wochiza, Wokwaniritsa Zonse, Msungi, Wokhululukira, Wachifundo chopambana.
- Bahá'u'lláh