Return to BahaiPrayers.net
Facebook
O Ambuye wanga, wokondedwa wanga, khumbo langa! Khalani bwenzi langa pamene ndili ndekha ndikundiperekeza Ine pamene ndathamangitsidwa kuchoka kwathu. Chotseleni chisoni changa. Ndipangeni kuti ndikhale wodzipereka kukukongola kwanu. Ndibwezeni kwa aliyense koma Inu Nokha. Ndikopeni kubzolera mkununkhira kwanu koyera. Ndipangeni kuti ndichezerane mu ufumu Wanu ndi iwo amene adzipatula ku zinthu zonse koma Inu Nokha, amene afunitsitsa kutumikira ku khomo Lanu lopatulika ndikuima kugwira ntchito mchiphunzitso Chanu. Ndipangeni ndikhale m’modzi wa adzakazi Anu amene afika ku chikondwerero Chanu. Indetu, Inu Ndinu Wachisomo, Wachaulere.
- `Abdu'l-Bahá