Return to BahaiPrayers.net
Facebook
O Mulungu! O Mulungu! Ino ndi mbalame yothyoka phiko ndipo kuwuluka kwake ndi kwapang’onopang’ono, ithandizeni kuti ithe kuwuluka kufika kunsonga ya chuma ndi chipulumutso, iwuluke ulendo wake ndi chimwemwe ndi chisangalaro chonse kunka mu mlengalenga mopanda malire, kwezani nyimbo yake m’Dzina Lanu Lalikulu mu zigawo zonse, sangalatsani makutu ndi kuyitanaku, ndikuwalitsa maso pakuwona zizindikiro za chitsogozo!
O Ambuye! Ndine m’modzi, ndekha, ndi wopepuka. Kwa ine kulibe mtsamiro wina uliwonse koma Inu Nokha, ndilibe mthandizi Ndinu Nokha ndipo ndilibe mtonthozi wina woposa Inu. Ndilimbikitseni mu ntchito Yanu, ndithandizeni kulankhula za nzeru Zanu pakati pa zolengedwa Zanu. Indetu, Inu Ndinu mthandizi wa ofooka ndi mtchinjirizi wa ang’onoang’ono, ndipo indetu, Inu Ndinu Wamphamvu, Wamkulu ndi Wosakakamizidwa!
- `Abdu'l-Bahá