Return to BahaiPrayers.net
Facebook
O Inu Mulungu Wosafaniziridwa! O Inu Ambuye wa Ufumu! Miyoyo iyi ndi ankhondo Anu akumwamba. Athandizeni iwo, ndipo ndi magulu Akhamu Lapamwamba Muwapambanitse; kuti yense wa iwo akhale ngati gulu la nkhondo ndi kugonjetsa maikowa kupyolera mu chikondi cha Mulungu ndi kuwala kwa uzimu kwa Chiphunzitso Chanu.
O Mulungu! Mukhale wowatchinjiriza ndi Mthandizi wao, ndipo m’chipululu, m’phiri, m’chigwa, m’nkhalango, m’madambo ndi m’nyanja, khalani Inu wowasangalatsa – kuti alire kupyolera mu mphamvu ya Ufumu ndi kuuzira kwa Mzimu Woyera!
Indetu, Inu Ndinu Wamphamvu, Wamkulu ndi Mwinimphamvu, ndiponso Inu Ndinu Wanzeru, Wakumva ndi Woona.
- `Abdu'l-Bahá