Return to BahaiPrayers.net
Facebook
O Mulungu wanga! O Mulungu wanga! Inu mukundiona ine mukutsika kwanga ndi kufooka kwanga, otanganidwa ndi ntchito yaikulu, ndikutsimikiza kukweza liwu Lanu pakati pa magulu a wanthu ndi kufalitsa ziphunzitso Zanu pakati pa anthu Anu. Ndingapambane bwanji popanda kuthandizidwa ndi Inu ndi kuuzira kwa Mzimu Woyera, ndithandizeni kuti ndipambane ndi makamu a ufumu Wanu wa ulumerero. Ndikundipatsa chitsimikizo Chanu chimene pachokha chikhoza kusintha kachilombo kakang’ono kwambiri koluma kukhala chiombankhanga, kadontho ka madzi kukhala mitsinje ndi nyanja ndipo kanthu kakang’ono kukhala kuwala ndi dzuwa?
Inu ndinu Wamphamvu ndi Wochita chilichonse chimene mufuna.
- `Abdu'l-Bahá