Return to BahaiPrayers.net
Facebook
Ulemelero ukhale kwa Inu, O Ambuye Mulungu wanga! Musanyasidwe naye iye amene Inu mwamkweza kupyolera mu mphamvu ya ufumu Wanu wamuyaya, ndi kumsiya kutali ndi Inu, amene Inu Munamlola kulowa m’chihema Chanu cha kunthawi zosatha. Kodi Mungamtaye, O Mulungu wanga iye amene Inu Mwamphimba ndi Ufumu Wanu ndipo mungamtembenukire, O chifuniro changa amene Mwakhala pothawira pake? Mungamunyoze iye amene Inu Mwamtukula, kapena Kumuiwala iye amene Inu munanthandiza kukukumbukirani? Wolemekezedwa, kwamtheradi Muli Wolemekezedwa Inu! Inu muli Amene kuyambira pachiyambi Mwakhala Mfumu ya chilengedwe chonse ndi Woyendetsa Wake ndipo mpaka ku nthawi zosatha Mudzakhalabe Ambuye wa zolengedwa zonse ndi Mkozi Wake.
Wolemekezedwa muli Inu, O Mulungu wanga! Ngati Muleka kuchitira chisoni antchito Anu, ndani nanga angawachitire chisoni? Ndipo ngati Mukana kudyetsa okondedwa Anu, kuli ndaninso woti angawadyetse? Wolemekezedwa, kwamtheradi Muli Wolemekezedwa
Inu! Inu Mulambiridwa m’choonadi Chanu, ndipo Inu ndithudi ife tonse tikupembedzani, ndipo Inu Muli woonekera m’chilungamo Chanu, ndipo kwa Inu tonse, ndithu tichitira umboni. Inu muli, mchoonadi, wokondedwa mchisomo Chanu. Palibe Mulungu wina koma Inu Wothandiza pa Tsoka, Wosasowa kanthu.
- Bahá'u'lláh