Return to BahaiPrayers.net   Facebook

Iye ndi Mulungu, ndi Iye Wokwezeka, Ambuye wokoma mtima ndi wa chaulere! Ulemelero ukhale kwa Inu, O Inu Mulungu wanga, Ambuye Mwini-mphamvu.

Ine ndichitira umboni ku Umwini-mphamvu Wanu, Ukulu Wanu, Ufumu Wanu, Kukomamtima Kwanu, Chisomo Chanu ndi Mphamvu Yanu, Umulungu Wanu, umodzi wa khalidwe Lanu, kupatulika Kwanu ndi kukwezeka Kwanu pamwamba padziko la chilengedwe ndi zonse ziri m’menemo.

O Mulungu wanga, Mukundiona ine ndadzipatula kuzinthu zonse koma kwa Inu, ndakakamira kwa Inu ndi kutembenukira kunyanja ya mphatso Zanu, kumwamba kwa chaulere Chanu, ku Nthanda ya Chisomo Chanu.

Ambuye! Ine ndichitira umboni kuti mwa wantchito Wanuyu munaikamo cholowa Chanu, ndiwo mzimu umene Inu Munapatsa nawo moyo kudziko lapansi.

Ndikupemphani kupyolera kwa Chibvumbulutso Chanu, mwa chifundo Chanu. Bvomerani zimene iye wazichita bwino m’masiku Anu. Mloleni chomwecho kuti abvekedwe ndi ulemelero wa ubwino Wanu ndi kuwalitsidwa ndi kulandilidwa Kwanu.

O Ambuye wanga, ineyo ndi zolengedwa zonse tichitira umboni kumphamvu Zanu ndi kukupemphani kuti musausiye mzimu uwu kutali ndi Inu umene wakwera kwa Inu, kumalo Anu akumwamba, ku Paradiso Wanu wokwezeka ndikumpumulo wofupikira kwa Inu.

O Inu amene Muli Ambuye wa anthu onse! Lolani tsono, O Mulungu wanga, kuti wantchito Wanuyu achezerane ndi osankhika Anu, Oyera Anu ndi Atumiki Anu m’malo a kumwamba amene cholembera sichingathe kunena kapena lilime kusimba.

O Ambuye wanga, wosaukayo wathamangiradi ku Ufumu wa chuma Chanu, mlendoyu wafika kwao mkati mwa mabwalo Anu, iye waludzu ku mtsinje wakumwamba wa chaulere Chanu. Musam’mane, O Ambuye gawo lake la phwando la chisomo Chanu ndi Chifundo cha chaulere Chanu. Inu zoonadi Ndinu Wamphamvu-zonse, Wachisomo, Wachaulere!

O Mulungu wanga cholowa Chanu chabwezedwa kwa Inu. Nkoyenera chisomo Chanu ndi chaulere Chanu zimene zazungulira ulamuliro Wanu mdziko lapansi ndi kumwamba, kupereka kwa yemwe Mwamlandira tsopanoyu mphatso Zanu ndi madalitso Anu, ndi zipatso za mtengo wa chisomo Chanu! Muli ndi mphamvu kuchita monga momwe Mufunira. Kulibe Mulungu wina koma Inu, Wachisomo, Wachaulere chodzaza, Wachisoni, Wopatsa, Wokhululukira,

Wamtengowapatali, Wodziwa-zonse.

Ndichitira umboni, O Ambuye wanga, kuti Inu Mwawafunsa anthu kulemekeza mlendo wao, ndipo yemwe wakwera kwa Inu wafikadi kwa Inu ndipo walandiridwa pamaso Panu. Chitanayeni chomwecho malinga ndi chisomo Chanu ndi chaulere Chanu! Mwaulemerelo Wanu, Ine ndidziwa kwa mtheradi kuti simudzakana chimene Inu mwawalamulira akapolo Anu kapena simudzam’mana iye amene wakakamira pa chingwe cha chaulere Chanu ndi kukwera ku kasupe wa chuma Chanu.

Kulibe Mulungu wina koma Inu, M,modzi Yekha, Wamphamvu, Waponse-ponse, Wachaulere.

 


English  
ភាសាខ្មែរ  
አማርኛ.  
Afrikaans  
Alaska Native  
American Indian  
Azərbaycan  
Bahasa Indonesia  
Bahasa Malaysia  
Bidayuh  
Bosanski  
Canadian Indigenous  
Català  
Cebuano  
Česky  
Chamorro  
Chichewa  
Corsica  
Cymraeg  
Daga  
Dansk  
Deutsch  
Dzongkha  
Eesti  
Español  
Esperanto  
Euskara  
Fiji  
Filipino  
Føroyar  
Français  
Frysk  
Hausa  
Hawaiian  
Hiri Motu  
Hrvatski  
Irish  
Íslenska  
Italiano  
Kabyle  
Kalaallisut  
Kiribati  
Kiswahili  
Kreyol Ayisyen  
Kuanua  
Kube  
Latviešu  
Lëtzebuergesch  
Lietuvių  
Luganda  
Magyar  
Malagasy  
Malti  
Māori  
Marshallese  
Melpa  
Montenegrin  
Nalik  
Namibia  
Nederlands  
Norsk  
Papiamentu  
Polski  
Português (BR)  
România  
Sámi  
Samoan  
Sarawak  
Sesotho  
Shqip  
Slovenščina  
Slovensky  
Sranan Tongo  
Srpski српски  
Suomi  
Svenska  
Tetum  
Tiếng Việt  
Tok Pisin  
Tongan  
Türkçe  
Türkmençe  
Tuvalu  
Vanuatu  
ελληνικά  
Беларускі  
български  
Кыргыз  
Монгол хэл  
Русский  
Тоҷикӣ  
Україна  
հայերեն  
اُردُو  
العربية  
فارسی  
नेपाली  
मराठी  
हिंदी  
বাংলা  
ગુજરાતી  
ଓଡ଼ିଆ  
தமிழ்  
తెలుగు  
ಕನ್ನಡ  
മലയാളം  
ภาษาไทย  
ພາສາລາວ  
한국어  
日本語  
简体中文  
繁體中文  
Windows / Mac