Return to BahaiPrayers.net
Facebook
(Pempheroli liyenera kugwiritsidwa kwa a Bahá’í okha amene ali ndi zaka zoyambila “Ndi pemphero lokhali lokakamiza la chiBahá’í limene limanenedwa pa gulu; liyenera kunenedwa ndi modzi mwa okhulupilira pamene onse abwerapo atayima…” –Kitáb-I-Aqdas)
O Mulungu wanga! Uyu ndi mtumiki Wanu ndi mwana wa mtumiki Wanu amene anakhulupirira Inu ndi zizindikiro Zanu, ndi kutembenukira nkhope yake kwa Inu, ndi kudzipatula kotheratu ku zonse koma Inu Nokha.
Inu zowonadi Ndinu mwa amene awonetsa chifundo wa chifundo chonse. Chitanayeni, O Inu Amene Mukhululukira machimo a anthu ndi kukwirira zoyipa zawo, monga momwe kufunikira m’mwamba mwa chaulere Chanu ndi nyanja ya chisomo Chanu. Mulowetseni kumalo a chifundo Chanu chachikulu amene analipo asanakhale maziko apansi ndi kumwamba. Kulibe Mulungu wina koma Inu Nokha, Wokhululukira Nthawi Zonse, wa Chaulere Chonse.
Onena pempheroli anene:
“Alláh-u-Abhá” (kamodzi)
Ife tonse, indetu, tipembedza Mulungu (19)
“Alláh-u-Abhá” (kamodzi)
Ife tonse, indetu, tigwada pamaso pa Mulungu (19)
“Alláh-u-Abhá” (kamodzi)
Ife tonse, indetu, tili wodzipereka kwa Mulungu (19)
“Alláh-u-Abhá” (kamodzi)
Ife tonse, indetu, tiyamika Mulungu (19)
“Alláh-u-Abhá” (kamodzi)
Ife tonse, indetu, tithokoza Mulungu (19)
“Alláh-u-Abhá” (kamodzi)
Ife tonse, indetu, tili ndi chipiriro mwa Mulungu (19)
Bahá’u’lláh
(Ngati womwalira ali mkazi, wonena pemphero anene: Uyu ndi mdzakazi Wanu ndi mwana wa mdzakazi Wanu………)
O Mulungu wanga! O Inu wokhululukira machimo, Wopereka mphatso, Wochotsa masautso! Indetu, ndikupemphani kukhululukira machimo a iwo amene asiya mayala a thupi ndi kukwera kudziko lauzimu.
O Mbuye wanga! Ayeretseni ku zoipa, achotsereni chisoni, ndipo sandulizani mdima wawo ukhale kuwala. Apangeni kulowa mmunda wa chimwemwe, atsukeni ndi madzi woyerayera, ndipo aloleni kuti awone kuwala Kwanu paphiri lalitali koposa.
- `Abdu'l-Bahá