Return to BahaiPrayers.net   Facebook

(Mapemphero ili limawerengedwa pa Manda a Bahá’u’lláh ndi Báb. Limagwiritsidwanso ntchito pokumbukira kubadwa kwa Bahá’u’lláh ndi Báb komanso kukumbukira kuwera kumwamba kwa Bahá’u’lláh ndi kuphedwa kwa Báb)

Mayamiko amene m’bandakucha wake waonekera ndi nkhope Yanu yolemekezeka kopambana, ndi ulemelero umene wawala kuchokera kwa Wokongola mowala kopambana, akhale pa Inu, O Inu Amene Muli Maonekedwe a Ulemelero, ndi Mfumu Yamuyaya, ndi Ambuye wa onse amene ali m’mwamba ndi padziko lapansi!

Ine nditsimikiza kuti kupyolera mwa Inu Ufumu wa Mulungu ndi Ukulu wa Mulungu ndi Ulemelero Wake, zinabvumbulutsidwa, ndipo nthanda za kunyezimira Kwake kwakale-kale zagwetsa kuwala kwao kumwamba kwa lamulo Lanu losasinthika, ndipo kukongola kwa Wosaonekayo kwawala pamwamba pa zolengedwa zonse.

Nditsimikizanso kuti ndi kuyenda kwa Cholembera Chanu Chokha, Chifuniro Chanu chakuti: “Khala Iwe” chakwaniritsidwa, ndiponso chinsinsi cha Mulungu chaululidwa, ndipo zinthu zonse zolengedwa zaitanidwa kumoyo ndi Zibvumbulutso zonse zatsika pansi.

Ine ndichitira umboninso, kuti kupyolera mwa kukongola Kwanu, Kukongola kwa Wopembedzayo kwaonetsedwa, ndipo kupyolera mwa Nkhope Yanu, Nkhope ya Wofunikayo Yawala, ndi kuti kupyolera mwa mau Anu, Inu mwaganizira bwino pakati pa zolengedwa zonse, kuwapangitsa amene ali wopembedza Inu kukwera ku nsonga ya ulemelero, ndi wosakhulupilira kugwera m’mbuna yakuya.

Ine ndichitira umboni kuti iye amene wakudziwani Inu wadziwa Mulungu, ndi iye amene wafika pamaso Panu wafika pamaso pa Mulungu. Chomwecho nkwakukulu kudalitsidwa kwa iye amene wakhulupilira mwa Inu, ndi mwa zizindikiro Zanu, ndipo walemekezedwa ndi kukomana Nanu, ndipo wafika pa zokoma za chifuniro Chanu, ndi kukuzungulirani ndi kuima patsogolo pa Mpando Wanu.

Tsoka kwa iye amene wakulakwirani Inu, ndipo wakukanani Inu, ndipo sanabvomera zizindikiro Zanu, ndipo watsutsa ufumu Wanu, ndipo wakuukirani Inu, ndipo wasonyeza kunyada pamaso Panu, ndipo wakangana ndi maumboni Anu, ndipo wathawa chilamulo Chanu ndi ulamuliro Wanu ndi kuwerengedwa limodzi ndi wosakhulupilira amene maina awo asindikizidwa ndi zala za kulamula Kwanu pamauthenga Anu oyera.

Chomwecho, uzirani kwa ine, O Mulungu wanga ndi Wokondedwa wanga, kuchokera kudzanja lamanja la chifundo Chanu ndi chisoni cha kukonda Kwanu, mphweya woyera wa ubwino Wanu, kuti zindichotse ine ndekha ndi m’dziko lapansi ndi kunditengera ku mabwalo a kuyandikira kwanu ndi pamaso Panu. Muli ndi mphamvu kuchita zomwe zakukomerani. Inu ndithudi Mwakhala Wamphamvu koposa zonse.

Chikumbukiro cha Mulungu ndi mayamiko Ache, ndi Ulemelero wa Mulungu ndi kuwala kwake zikhale pa Inu, O Inu Amene Muli kukongola Kwake! Ndichitira umboni kuti diso la chilengedwe silinaone wina wolakwiridwa monga Inu. Munamizidwa masiku onse amoyo Wanu pansi pa nyanja ya zowawa. Pa nthawi yina Munali m’maunyolo ndi nsinga; pa nthawi yinanso Munaopsezedwa ndi lupanga la adani Anu. Komabe, ngakhale ziri chomwecho munalamulira wanthu onse kutsata zonse zimene Munalangizidwa ndi Iye Amene Ali Wodziwa Zonse, Wanzeru Zonse.

Lolani mzimu wanga ukhale nsembe chifukwa cha zolakwa zimene Inu Munabvutika nazo ndi moyo wanga ukhale chopereka chifukwa cha mikwingwirima yomwe Munapwetekedwa nayo. Ndipempha Mulungu,mwa Inu ndi mwa iwo amene nkhope zawo zawalitsidwa ndi kuunika kwa Nkhope Yanu, ndi iwo amene, chifukwa cha chikondi Chanu, atsata zonse zimene anafunsidwa, kuchotsa zophimba zomwe zabwera pakati pa Inu ndi zolengedwa Zanu, ndi kundipatsa ine zabwino padziko lino ndi dziko lirinkudza. Inu zoonadi Ndinu

Wamphamvu Zonse, Wam’mwamba-mwamba, Woyerayera, Wokhululukira Nthawi Zonse, Wachifundo Chozama.

Dalitsani, O Ambuye Ambuye wanga, Mtengo Wopatulika wa Lote ndi masamba ake, ndi makungwa ake ndi nthambi zake, ndi misinde yake ndi mphukira zake malingana ndi momwe maina Anu opambana adzakhalira ndi maudindo Anu wotchuka kwambiri adzatha. Uchinjilizeni chomwecho kuchokera ku zokhumudwitsa za achiwembu ndi magulu ankhanza.

Inu Ndinu, zoonadi Wamphamvu Zonse, Wolimba Kwambiri. Dalitsaninso, O Ambuye Mulungu wanga, antchito Anu ndi adzakazi Anu amene afika kwa Inu. Inu zoonadi Ndinu Wachifundo Chonse, amene chisomo Chake m’chamuyaya. Palibe Mulungu wina koma Inu, Wokhululukira-nthawi Zonse, Wokomamtima.

 


English  
ភាសាខ្មែរ  
አማርኛ.  
Afrikaans  
Alaska Native  
American Indian  
Azərbaycan  
Bahasa Indonesia  
Bahasa Malaysia  
Bidayuh  
Bosanski  
Canadian Indigenous  
Català  
Cebuano  
Česky  
Chamorro  
Chichewa  
Corsica  
Cymraeg  
Daga  
Dansk  
Deutsch  
Dzongkha  
Eesti  
Español  
Esperanto  
Euskara  
Fiji  
Filipino  
Føroyar  
Français  
Frysk  
Hausa  
Hawaiian  
Hiri Motu  
Hrvatski  
Irish  
Íslenska  
Italiano  
Kabyle  
Kalaallisut  
Kiribati  
Kiswahili  
Kreyol Ayisyen  
Kuanua  
Kube  
Latviešu  
Lëtzebuergesch  
Lietuvių  
Luganda  
Magyar  
Malagasy  
Malti  
Māori  
Marshallese  
Melpa  
Montenegrin  
Nalik  
Namibia  
Nederlands  
Norsk  
Papiamentu  
Polski  
Português (BR)  
România  
Sámi  
Samoan  
Sarawak  
Sesotho  
Shqip  
Slovenščina  
Slovensky  
Sranan Tongo  
Srpski српски  
Suomi  
Svenska  
Tetum  
Tiếng Việt  
Tok Pisin  
Tongan  
Türkçe  
Türkmençe  
Tuvalu  
Vanuatu  
ελληνικά  
Беларускі  
български  
Кыргыз  
Монгол хэл  
Русский  
Тоҷикӣ  
Україна  
հայերեն  
اُردُو  
العربية  
فارسی  
नेपाली  
मराठी  
हिंदी  
বাংলা  
ગુજરાતી  
ଓଡ଼ିଆ  
தமிழ்  
తెలుగు  
ಕನ್ನಡ  
മലയാളം  
ภาษาไทย  
ພາສາລາວ  
한국어  
日本語  
简体中文  
繁體中文  
Windows / Mac