Return to BahaiPrayers.net
Facebook
Ndadzuka m’mawa uno ndi chisomo Chanu, O Mulungu wanga, ndikunyamuka pakhomo panga ndi kukhulupirira kotheratu mwa Inu, ndi kudzipereka ndekha ku chisamaliro Chanu. Tumizani tsono, pa ine, kuchokera ku mwamba kwa chifundo Chanu, madalitso ochokera kwa Inu, ndipo Mundilole ndibwerere kwathu bwino monga momwe Munandilolera kunyamuka muchitetezo Chanu, ndi maganizo anga onse ali pa Inu. Kulibe Mulungu wina koma Inu Nokha, M’modzi Yekha, Wosafanizilika, Wodziwa Zonse, Wanzeru Zonse.
- Bahá'u'lláh