Return to BahaiPrayers.net
Facebook
O Mulungu, Mulungu wanga! Ndanyamuka pa khomo langa, kugwiritsitsa chingwe cha chikondi Chanu, ndipo ndadzipereka ndekha kwathuthu ku chisamaliro Chanu ndi chitetezo Chanu. Ndikupemphani Inu ndi mphamvu Yanu imene Inu mwateteza nayo okondedwa Anu ku zopinga ndi makhalidwe oipa, ndi kwa ankhanza ndi achiwembu amene akhala kutali ndi Inu, nditetezeni ine ndi mphatso Zanu ndi chisomo Chanu. Ndiloleni, tsono, ndibwerere kwathu ndi mphamvu Zanu ndi nyonga Zanu.
Inu, Choonadi, Wamphamvu Zonse, Wothandiza pa Tsoka, Wodzidalira Nokha.
- Bahá'u'lláh