Return to BahaiPrayers.net
Facebook
O Mulungu wanga! O Mulungu wanga! Lumikizani mitima ya antchito Anu, ndipo Muwaululire iwo cholinga Chanu Chachikulu. Aloleni iwo atsate malangizo Anu ndi kusunga malamulo Anu. Athandizeni iwo, O Mulungu, mukuyesetsa kwao, ndipo muwapatse mphamvu kuti akutumikireni Inu. O Mulungu, Musawasiye iwo mwa iwo okha, koma mutsogoze mapazi awo ndi kuwala kwa nzeru Zanu ndipo sangalatsani mitima yawo ndi chikondi Chanu. Indetu, Inu Ndinu Mthandizi wawo ndi Mbuye wawo.
- Bahá'u'lláh