Return to BahaiPrayers.net
Facebook
Ulemelero ukhale kwa Inu, O Mulungu, chifukwa chakuwonetsa chikondi Chanu kwa mtundu wa anthu! O Inu Amene Muli Moyo wathu ndi Kuwunika kwathu, tsogolereni a ntchito Anu mu njira Yanu, ndipo mutipatse kukhala wolemera mwa Inu ndi kukhala omasuka ku ziri zonse kupatula Inu Nokha.
O Mulungu, Tiphunzitseni Umodzi Wanu ndipo Mutipatse kuzindikira Mgwirizano Wanu, kuti tisawone aliyense koma Inu Nokha. Inu Ndinu Wachifundo ndi Wopatsa Chaulere. O Mulungu, Lengani m’mitima ya wokondeka Anu moto wa chikondi Chanu, kuti utenthe maganizo a chirichonse kupatula a Inu Nokha.
Tiululireni, O Mulungu, Ukulu Wanu wosatha-kuti Inu mudalipo ndipo mudzakhalapobe nthawi zonse, ndipo kuti kulibenso Mulungu wina koma Inu Nokha. Indetu, mwa Inu tidzapeza chitonthozo ndi mphamvu.
- Bahá'u'lláh