Return to BahaiPrayers.net
Facebook
55. O Inu amene mayesero Ake ndi mankhwala ochiritsa kwa iwo amene ali pafupi Nanu, lupanga Lake liri chifuniro chopambana cha onse amene akukondani Inu, mubvi Wake ndi pempho lapamtima la mitima ya iwo amene akuzindikira choonadi Chanu! Ndikupemphani, mwa kukoma Kwanu kwa uzimu ndi kunyezimira kwa ulemelero wa nkhope Yanu, kuti Mutitumizire ife kuchokera ku malo Anu m’mwamba chimene chingatipangitse ife kuyandikira kwa Inu.
Choncho Limbikitsani mapazi athu, O Mulungu wanga M’Chiphunzitso Chanu, ndipo Walitsani mitima yathu ndi kuwala kwa nzeru Zanu, ndipo Unikirani m’zifuwa zathu ndi kuunika kwa Maina Anu.
- Bahá'u'lláh