Return to BahaiPrayers.net
Facebook
Iye ndi Wachisoni, Wachaulere Chonse! O Mulungu,
Mulungu wanga! Inu mukundiwona ine, Inu mukundidziwa ine; Inu amene muli Panthunzi panga ndi
Pothawira panga, Palibe amene ndasankha kapena kufufuza kupatula Inu, palibe njira yomwe ine ndayendamo kapena kufuna kudzayenda koma mnjira Yanu ya chikondi Chanu.
Mu mdima wa ndiwe yani wa mabvuto, maso anga amatembenukira ndi oyembekezo ndi odzadzidwa ndi chikhulupiriro ku m'mawa wa chifundo Chanu chopanda malire ndipo ora la m’bandakucha mzimu wanga wofoka umatsitsitmutsidwa ndi kulimbikitsidwa pokumbukira kukongola Kwanu ndi ungwiro Wanu. Iye amene chisomo cha chifundo Chake chamuthandiza, ngakhale kuti katakhala kadontho kakang’ono, kadzasanduka nyanja yopanda malire, ndipo kanthu kochepetsetsa kamene kathandizidwa ndi chifundo Chake, kadzawala ngati nyenyezi lowalitsitsa.”
“Khalani pansi pa chitetezo Changa, O Mzimu Wanga wa chiyero, Inu amene muli Opereka Zaulere Zonse, wantchito Wanu uyu wokondedwa ndi, wowalitsidwa. Muthandizeni mu dziko ili la umunthu kuti akhale osagwedezeka ndi olimba mu chikondi Chanu ndipo mpatseni iye amene ali mbalame yothyoka phiko kuti apeze pothawira ndi mthuzi wa chisa Chanu cha uzimu chimene chakhazikika pa mtengo wa kumwamba.”
- `Abdu'l-Bahá