Return to BahaiPrayers.net
Facebook
O Mulungu! Tsitsimutsani ndi kusangalatsa mzimu wanga. Yeretsani mtima wanga. Walitsani mphamvu zanga. Ndikupereka zanga zonse m’dzanja Lanu. Inu ndiye Chitsogozo changa ndi Pothawira panga. Sindidzakhala wachisoni ndi wokhumudwa; Ndidzakhala munthu wokondwa ndi wosangalala. O Mulungu! Sindidzakhalanso ndi nkhawa, kapena kulola mabvuto kundigonjetsa. Sindidzakhala pa zinthu zosakondweretsa moyo.
O Mulungu! Inu Ndinu bwenzi langa kwa ine kuposa m’mene ndiri ine kwa ine mwini. Ndikudzipereka kwa Inu, O Ambuye.
- `Abdu'l-Bahá