Return to BahaiPrayers.net
Facebook
O Ambuye! Ndife wofooka; tilimbikitseni. O Mulungu! Ndife mbuli; tipangeni kukhala wozindikira. O Ambuye! Ndife amphawi; tipangeni kukhala wolemera. O Mulungu! Ndife akufa; titsitsimutseni. O Ambuye! Ndife wosayenerezeka konse; tipatseni ulemerero mu ufumu Wanu. Ngati mutithandiza, O Ambuye, tidzakhala ngati nyenyezi zothwanima. Ngati simutithandiza, tidzakhala wotsika kuposa dziko lapansi limene.
O Ambuye! Tilimbikitseni. O Mulungu! Tipatseni kupambana. O Mulungu! Tithandizeni kugonjetsa kudzikonda ndi chilakolako. O Ambuye! Tipulumutseni ku nsinga za dziko lapansi. O Ambuye! Titsitsimutseni kupyolera mu kuuzira kwa Mzimu Woyera kuti tsono tithe kuchilimika ndi kukutumikirani, kukupembedzani, ndikudzipereka kwa thunthu mu ufumu Wanu ndi chikhulupiriro chonse.
O Ambuye! Inu Ndinu Wamphamvu! O Mulungu, Inu
Ndinu Wokhululukira! O Ambuye, Inu Ndinu
Wosamalira!
- `Abdu'l-Bahá