CHIKHULULUKIRO (#13455)

O Inu Wamphamvu zonse! Ine ndine wochimwa, koma Inu Ndinu Wokhululukira! Ine ndiri wosakwanira, koma Inu muli wachisoni! Inde ndiri mumdima wa uchimo koma Inu Ndinu nyali ya Chikhululukiro! O Inu Mulungu Wachifundo! Khululukirani machimo anga, ndipatseni mphatso Zanu, iwalani mphulupulu zanga, ndichinjirizeni ndi kundimiza m’kasupe wa chipiliro Chanu ndipo ndichizeni ine kudwala konse ndi matenda.  
Ndiyeretseni ndi kundidalitsa ndipo ndipatseni gawo kuchokera ku mbvumbi wakuyera, mwakuti chisoni ndi kusakondwa zichoke ndipo chisangalalo ndi chimwemwe zitsike. Lolani kuti nkhawa ndi makaiko zisanduke kukondwa ndi kukhulupirira ndipo bvomerani kuti kulimba mtima kulowe m’malo mwa mantha.  
Ndithudi, Inu Ndinu Wokhululukira, Wachisoni, ndipo Ndinu Waufumu ndi Wokondeka.

-`Abdu'l-Bahá
-----------------------

