CHITETEZO (#13456)

O Ambuye wanga! Inu Mudziwa kuti wanthu azunguliridwa ndi zowawa ndi matsoka ndipo adzazidwa ndi zolemetsa ndi mabvuto. Yeso lirilonse limtsata munthu ndipo chobvuta chilichonse chikumlonda ngati kuluma kwa njoka. Palibe tchinga ndi pothawira kwa iye koma pansi pa phiko la chitetezo, kusamala, kulonda ndi kusunga Kwanu.  
O Inu Wachifundo, O Ambuye wanga! Konzani chitetezo Chanu chikhale chida changa, kusamala Kwanu chishango changa kudzichepetsa pakhomo la umodzi Wanu mlonda wanga, ndikusunga Kwanu ndikutchinga Kwanu linga langa ndipokhala panga. Ndisamalireni ine ku maganizo anga ndi zofuna zanga ndipo Ndilanditseni ku matenda, mayesero, mabvuto ndi masautso. Ndithudi, Inu Ndinu Mtetezi, Mchinjirizi, Msungi, Wokwaniritsa, ndipo ndithudi, Inu Ndinu Wachifundo wa achifundo Chopambana.

-`Abdu'l-Bahá
-----------------------

