CHITHANDIZO (#13457)

O Mulungu wanga! Ndikupemphani, kubzolera mdzina Lanu la Ulemelero, kundithandiza mu zimene zingapange ntchito za atumiki Anu kupita patsogolo, ndikukulitsa mizinda Yanu. Inu indetu, muli ndi mphamvu pazinthu zonse!

-Bahá'u'lláh
-----------------------

CHITHANDIZO (#13458)

Ambuye! Ife ndife womvetsa chisoni, tipatseni chifundo Chanu; ndife wosauka, tipatseni gawo kuchokera ku nyanja ya chuma Chanu; ndife wosowa, tikwaniritseni; wosayenera, tipatseni ulemelero Wanu. Mbalame zamlengalenga ndi nyama za mu thengo zimalandira zakudya zawo tsiku ndi tsiku kuchokera kwa Inu ndipo za moyo zonse zimalandira chisamaliro ndi chikondi Chanu. Musam’mane wofookayu chisomo Chanu chodabwitsa ndipo gwetselani mwa mphamvu Yanu madalitso Anu akulu pamzimu wobvutikawu.  
Tipatseni ife chakudya chathu chalero ndi zofunikira za moyo wathu, kuti tisadalire pa aliyense koma Inu Nokha, tigwirizane kotheratu ndi Inu, tiyende munjira zanu ndi kuwuza anthu za kudabwitsa Kwanu. Inu Ndinu Wamkulu ndi Wachikondi ndi amene Mupereka kwa mtundu wonse wa anthu.

-`Abdu'l-Bahá
-----------------------

