KUDZIPEREKA (#13465)

Mulungu pangeni kukhala bango la Mphako, mmene thima la kudzikonda lakolokotedwamo, tsono kuti ndi khale mphako yoyera mmene chikondi Chanu chingadutsire popita kwa ena. Ndasiya mbuyo mwanga kusadekha ndi kusakhutira. Ndidzipereka ndekha kwa thunthu mmanja Mwanu, pakuti Ndinu Chitsogozo Changa mchipalamba, Mphunzitsi wa umbuli wanga. Sing'anga wa nthenda yanga. Ndine msilikali mgulu la nkhondo la Mfumu yanga, ndapereka chifuniro changa kwa Iye ndi moyo wanga-kuti Achite nawo mmene Iye Afunira. Sindidziwa tsogolo ndi lotani mwandikonzera ine, ndiponso sindifuna kufufunza kapena kufuna kudziwa. Tchito m'tsiku indikwanira ndipo tsogolo lonse liri Lanu.  
Pang'ono ndi pang'ono Inu musintha kufooka kukhala nyonga, kukaika kukhala kukhulupirira, kusokonezeka kukhala kumvetsetsa. Pomwe ndi oyenera kusenza chipsinjo, Inu Muchiyedzeka pa phewa langa. Pamene ndakonzeka kulowa m'thengo, Inu Mundipatsa malo m’gulu la nkhondo la kuwala. Tsopano ndiribe ntchito ina yoposa kumvala zirimbe muntchito Yanu. Ndi kufunitsitsa ndiponso kudekha, ndi chiyembekezo ndiponso kuthokoza ndi weramira ku ntchito ya ora lino, kuopa kuti; pamene kuitana Kwanu kudza ndingapezeke osakonzeka.

-`Abdu'l-Bahá
-----------------------

