KULIMBIKIRA (#13466)

O Ambuye Mulungu Wanga! Thandizani wokondedwa Anu kukhala wolimba m’chikhulupiliro chanu, kuyenda munjira Zanu, ndikukhala wochilimika mu ntchito Yanu. Apatseni chisomo Chanu kuti athe kulimbana ndi zilakolako zawo, kutsata kuwala kwa chitsogozo chauzimu. Inu Ndinu Wamphamvu, Wachisomo, Wodzidalira Nokha, Wopereka Madalitso, Wachikondi, Wamkulu, Wachaulere Chonse.

-`Abdu'l-Bahá
-----------------------

