KUYAMIKA (#13470)

Likuzike Dzina Lanu, O Ambuye Mulungu wanga! Inu ndi Iye amene zinthu zonse zimpembedza ndi Amene sapembedza kanthu. Amene Ali Ambuye wa zinthu zonse ndipo Sali kapolo wa kanthu. Amene Adziwa zonse koma sadziwidwa ndi kanthu. Inu Munafuna kuzizindikiritsa Nokha kwa wanthu; choncho, kupyolera mwa liu lapakamwa panu munadzetsa chilengedwe ndi kupanga m’mwamba. Palibe Mulungu wina koma Inu Nokha, Mkozi, Mulengi, Wamkulukulu, Wamphamvu Zonse.  
Ndikupemphani, mwa liu lomweli, limene lawala pamwamba pa mzere wa Chifuniro Chanu, mundilore ndimwe mokwanira, madzi amoyo amene mwatsitsimutsa nawo mitima ya wosankhidwa Anu ndi kuukitsa mizimu ya wokondedwa Anu, kuti ine nthawi zonse, m’zooneka zonse, nditembenukire nkhope yanga kwa Inu.  
Inu Ndinu Mulungu Wamphamvu, Waulemelero ndi Chaulere. Kulibe Mulungu wina pambali Panu, Woweruza Wamkulu, Woyerayera, Wanzeru-zonse.

-Bahá'u'lláh
-----------------------

