MSONKHANO (#13472)

Inu Ambuye wachifundo! Awa ndi antchito Anu amene akumana mu msonkhano uno, atembenukira ku ufumu Wanu ndipo akusoweka mpatso ndi madalitso Anu. O Inu Mulungu! Mvumbulutsani ndi kuwonetsa zizindikiro za umodzi Wanu zimene zaikidwa mu za moyo zonse.  
Mvumbulutsani ndi kuwonetsa makhalidwe amene Inu mwawaika mwa anthuwa. O Mulungu! Ife tili monga zomera, ndipo mphatso Yanu ili monga mvula; tsitsimutsani ndi kupanga zomerazi kukula kupyolera mu mphatso Zanu. Ife ndi antchito Anu; tipulumutseni ku zinthu za dziko. Ndife mbuli; tipangeni kukhala ozindikira. Ndife akufa; tipangeni tikhale a moyo. Ndife okonda zinthu zopanda pake; tipatseni mzimu. Ndife omanidwa; tipangeni tikhale olandila zodabwitsa Zanu. Ndife osowa; tilemeletseni ndi kutidalitsa kuchokera ku chuma Chanu chopanda malire.  
O Mulungu! Titsitsimutseni ife, tipatseni ife maso; tipatseni ife makutu; tidzazeni ife ndi zodabwitsa zamoyo, choncho kuti zobisika za ufumu Wanu ziwululidwe ndipo tidzikhuthule ku umodzi Wanu. Mphatso iliyonse imachokera kwa Inu; pemphero lirilonse ndi Lanu.  
Inu ndinu Wanyonga. Inu Ndinu Wamphamvu. Inu Ndinu Wopatsa, ndipo Inu ndi Wachaulere nthawi zonse.

-`Abdu'l-Bahá
-----------------------

