M’MAWA (#13442)

Ndauka mu chifungatiro Chanu, O Mulungu wanga, ndipo ndikoyenera kwa iye wofuna chifungatirocho kukhalamo mu Malo Oyera a chitetezo Chanu ndi mu Tchinga la linga Lanu. Walitsani m’kati mwanga, O Ambuye wanga, ndikuwala kwa m’bandakucha wa Chibvumbulutso Chanu, monga momwe mudawalitsa thupi langa ndi kuwala kwa m’mawa wa chaulele Chanu.

-Bahá'u'lláh
-----------------------

