PANGANO (#13477)

O Mulungu, Mulungu wanga! Atchingireni atumiki Anu wokhulupirika ku zoyipa za kudzikonda ndi dama, atetezeni ndi kulondera kwa diso la chikondi Chanu ku zopinga zonse, udani ndi dumbo, asungeni mlinga lolimba la chisamaliro Chanu ndipo, asakhale wokayika, apangeni kukhala zitsanzo za zizindikiro za ulemerero Wanu, walitsani nkhope zawo ndi kuwala kopambana kochokera ku m’bandakucha wa umodzi Wanu wa uzimu, sangalatsani mitima yawo ndi malemba omwe aululidwa kuchokera mu ufumu Wanu woyera, limbikitsani mafupa awo ndi mphamvu zanu zokokolora zodzera kumwamba kwa ulemerero Wanu. Inu Ndinu wa Chaulere Chonse, Mtetezi, Wamkulu, Wachisomo.

-`Abdu'l-Bahá
-----------------------

