UKWATI (#13483)

Ulemelero ukhale kwa Inu, O Mulungu wanga! Indetu, wantchito Wanuyu ndi mdzakazi Wanuyu asonkhana pansi pa m’thunzi wa chifundo Chanu ndipo agwirizana kubzolera muchifundo ndi kuolowa manja Kwanu. O Ambuye! Athandizeni iwo m’dziko Lanu lino ndi Muufumu Wanu ndipo akonzeleni iwo zabwino zonse kubzolera mu chaulere ndi chisomo Chanu.  
O Ambuye! Alimbikitseni iwo mkukutumikirani ndipo athandizeni mu ntchito Yanu. Muwapange iwo kukhala zizindikiro za Dzina Lanu mdziko Lanu ndipo atetezeni iwo kubzolera mu mphatso Zanu zimene siziguga mu dziko lino ndi mu dziko lirinkudza. O Ambuye! Iwo akupempha ku Ufumu wa chifundo Chanu ndi kuyitana ku ufumu wa Nokha Wanu.  
Indedi, akwatirana pakumvera lamulo Lanu. Apangeni iwo kukhala zizindikiro za kumvana ndi umodzi kufikira kutha kwa nthawi. Indedi Inu Ndinu Wanyonga Zonse, Waponseponse ndi Wamphamvu Zonse!

-`Abdu'l-Bahá
-----------------------

