Return   Facebook

The Universal House of Justice

Ridván 2022

To the Bahá’ís of the World

Dearly loved Friends,

Chaka cha kukonzekera ndi kuwunikira, komanso cha kuyesetsa kwakukulu, chafika kumapeto, chopatulika ndi kuyesetsa kwa abwenzi pa dziko lonse kukwaniritsa zaka zana limodzi (100) za kukwera kumwamba kwa ‘Abdu’l-Bahá, kuphatikizapo kutumiza nthumwi kukatenga nawo gawo pa kukumana kwapadera kukumbukira Iye ku Malo Woyera. Kudzera mu kuyesetsa kumeneku, chilimbikitso choperekedwa ndi moyo wa ‘Abdu’l-Bahá chakhudza mizimu yosawerengeka osati ya a Baha’i okha. Kukhudzika kwake pa membala aliyense wa mtundu waanthu, ntchito Yake yophunzitsa, Kutukula kwa ntchito za maphunziro ndi moyo wabwino Kwake, zosonkhera Zake zazikulu ku ntchito zakum’mawa ndi kumadzulo, Chilimbikitso Chake chochokera pansi pamtima pa ntchito zomanga Nyumba Zopembedzeramo, kuthandizira kwake kukhazikitsa zikhazikitso za chiBaha’i za kayendetsedwe, kusonkhanitsa kwake kwa mbali zosiyana-siyana za moyo wa mbumba – zonse izi zoyimira moyo Wake zina Chikumbutso cha kudzipereka kwake kotheratu ndi kopitilira ku kutumikira Mulungu ndi kutumikira mtundu wa anthu. Pamwamba pokhala chiphona cha kutsogolera kwa khalidwe labwino ndi kupambana ziphunzitso zauzimu, ‘Abdu’lBahá anali chodutsiramo changwiro momwe mphamvu yotulutsidwa ndi Chibvumbulutso cha Bahá’u’lláh ingagwilire ntchito pa dziko lapansi. Pofuna kumvetsa mphamvu yomanga dera yomwe ili mu Chipembedzochi, munthu sakufunika kuyang’ananso kwina koma ku zipambano za ‘Abdu’l-Bahá mu nthawi ya utumiki Wake ndi mphamvu zosintha za chitsogozo zomwe zinatuluka mosalekeza kuchokera ku cholembera Chake. Zambiri mwa zipambano zodabwitsa zomwe zikuchitika ndi mbumba ya chiBaha’i yalero – zomwe zinakambidwa m’mauthenga athu kwa inu mu Rizwani yapita – ikukhudza ku chiyambi cha ntchito, ziganizo ndi chitsogozo za

‘Abdu’l-Bahá.

Ndikoyenera bwanji, choncho, kuti chikumbukiro chapamodzi cha mbumba yachiBahá’í kwa Chitsanzo changwiro ichi chikhalenso chiyambi cha kuyambika kwa ntchito yayikulu yolunjika pa kutulutsa kwa mphamvu yomanga dziko ya Chipembedzo pa milingo yayikulu koposa. Mbali za ntchito yomwe ili m’gulu ili la Pulani ya Zaka Zisanu ndi Zinai (9), ndinso mu mndandanda wa Mapulani, zikulunjika ku chikwaniritso cha cholinga ichi chachikulu. Likhalanso thima la misonkhano yoposa 10,000 yomwe ikuchitika padziko lonse lapansi kupanga chiyambi cha ntchito iyi yauzimu yayikulu. Misonkhano iyi, yomwe ikuyembekezera kudzalandira chiwerengero chochuluka cha otenga mbali, ikubweretsa pamodzi osati aBahá’í okha komanso ena ofunira zabwino mtundu wa anthu amene ali ndi chidwi chobweretsa umodzi ndi kupanga dziko kukhala labwino. Kuchilimika kwawo ndi cholinga chawo chachikulu zikuonekera mu uzimu wopezeka mu misonkhano imene yachitika kale, komwe otenga mbali apatsidwa mphamvu kwambiri ndi zokambirana zosiyana-siyana zomwe iwo asonkhera ngati okhala ndi masomphenya apamodzi omwe anawunikidwa ku zochitika zosangalatsa zimenezi. Tikuyang’anira ndi chidwi ku zimene zituluke m’miyezi ndi mzaka zikubwerazi.

Chiperekereni uthenga wathu wapa 30 Disembala 2021 ku msonkhano wa Alangizi, maBungwe Aakulu Auzimu ndi Khonsolo za Mzigawo zachiBaha’i akhala akuwunguza mowona mtima kuthekera kochulukitsa ndondomeko za kukula m’makalasita a m’malire awo mkati mwa Pulani ya Zaka 9. Tikuona kuti zikhala zothandiza, ndicholinga choyesa chitsogolo chomwe chingachitike pakupita kwa nthawi, kuunikanso Pulani pomwe ikutambasuka m’magawo awiri a zaka zinayi (4) ndi zisanu (5), ndipo Mabungwe Aaukulu anafunsidwa kuganizira mtunda umene akuganizira kuwona, mu mbumba zawo pofika Rizwani 2026 kenako Rizwani 2031. Ntchito iyi inakhudzanso kuwunikiranso kwa malire a makalasita, zotsatira za kuwunika kumeneku ndi kwakuti chiwerengero chonse cha makalasita padziko lonse chakwera ndi theka la theka (kota) ndipo tsopano chili pa 22,000. Kutengera malipoti omwe alandiridwa, pali chiyembekezo choti, pofika mapeto a Pulani, pologalamu ya kukula yomwe ili pamtunda wina wake wopita chitsogolo idzapezeka m’makalasita osachepera 14,000 a makalasita onse. Kuchokera mwa amenewa, momwe pologalamu ya kukula idzakhala yafika pa kathithi chiwerengero chitha kuzakwera kufika pa 11,000 mu nthawi yomweyi. Ndipo mwa awa, pali chiyembekezo kuti chiwerengero cha makalasita amene adutsa mtunda wachitatu chidzakwera kudutsa 5,000 pofika 2031. Popanda kukayika, kuti mtunda umenewu udzakwaniritsidwe zikutanthauza kuyesetsa kwakukulu mu Pulani yonse. Koma tikuona kuti awa ndi magolo oyenera kuti tiyesetse kuwafikira, pakuti akuyimira ntchito yayikulu koma yofikirika.

Uku ndi kunena. Zolinga zotere sizikanakhala zoona ndi kuzilingalira pakanakhala kuti zikhazikitso za kayendetsedwe nazo sizinapite patsogolo mowonekeratu, kudzoza izo ndi kuthekera kwakulu kukwaniritsa zochita-chita za mbumba imene ntchito zake zachulukitsidwa mofulumira, kukhudza chiwerengero chopitilira kukula cha mizimu yogwirizana. Sizikanatheka kulakalaka kukula kotere ngati khumbo lofuna kuphunzira – kuchita, kuwunikira, ndi kupeza ziphunzitso, ndi kutenga zophunziridwa zotuluka malo ena – silikanapezeka pa milingo yonse, kufikira kumadera ammidzi ku mbumba. Ndipo kuyesetsa komwe chithuzi-thuzi ichi chikuyimira sikukanakhala kotheka potenga ntchito ya ndondomeko pophunzitsa ndi kusula anthu m’dziko lachiBahá’í. Zonsezi zabweretsa kupita patsogolo kwina kwake mu kuzindikira kwa mbumba yachiBahá’í pa cholinga ndi umunthu wake. Chidwi choyang’ana zinthu zina zozungulira mu ndondomeko yomanga dera chinali chitakhazikitsidwa kale mu zikhalidwe za madera ochuluka; ndipo tsopano yapereka zipatso, mu mbumba zochuluka zomwe zikudzuka, mu udindo weni-weni pa kupita patsogolo muuzimu ndi kuthupi kwa magulu akulu-akulu a anthu a m’madera, kufikira anthu ena osakhala aBahá’í. Kuyesetsa kwa abwenzi kamanga mbumba, kutenga mbali pa ntchito ya chitukuko cha m’madera, ndi kusonkhera ku ntchito zosiyana-siyana za’mdera zakhala ntchito imodzi yadziko lonse, yomangidwa pamodzi ndi ndondomeko yapamodzi yogwilira ntchito, yolunjika pa kuthandiza mtundu wa anthu kukhadzikitsa zinthu zake pa maziko a mfundo zauzimu. Kupatulika kwa zitukuko zomwe tafotokoza, kufikira apa zaka 100 chikhadzikitsireni Ndondomeko ya Kayendetsedwe, sikungayiwalidwe. Mu kukwera kodabwitsa kwa kuthekera kumene kwaoneka m’zaka nakumi awiri zapitazo – ndipo zomwe zapangitsa kuthekera kuti dziko lachiBahá’í liwunikira ntchito zake potengera mphamvu zotulutsidwa zomanga madera za Chipembedzo –tikuona umboni wokwanira kuti Chipembedzo cha Mulungu chalowa mu ndime yachisanu ndi chimodzi ya Kumanga (Formative Age). Tinalengeza mu Rizwani yapita kuti kufalikira kodabwitsa pa kutenga mbali kwa chiwerengero chochuluka mu zochitika-chitika zachiBahá’í, koyatsidwa ndi chikhulupiliro, ndi kupeza maluso ndi kuthekera koti atumikire madera awo kunaonetsa kuti gawo lachitatu la Pulani Yoyera ya Abdu’l-Baha inayamba; Pulani Ya Chaka Chimodzi, poyambilira pake kenako tsopano kumapeto, yayambitsa mbiri ya kutukuka komwe kwachitika ndi gulu la okhulupilira. Ndipo pachiyambi cha ntchito yatsopano yayikulu, thupi ili logwirizana la okhulupilira layima mokonzeka kutenga mwayi omwe watsegulidwa kwa ilo.

Chizindikiro chowonekeratu cha gawo lomwe tsopano likufika pamapeto linali kumanga kwa Nyumba Yopembedzera yomaliza ndi kuyambika kwa mapolojekiti wokhazikitsa Nyumba Zopembedzera m’maiko komanso m’zigawo za m’maiko. Zambiri zaphunziridwa, ndi aBaha’i padziko lonse, zokhudza Nyumba Zikuluzikulu Zopemphereramo (Mashriqu’l-Adhkár) ndi mgwirizano wa kupembedza ndi kutumikira komwe imayimira. Mkati mwa gawo la chisanu ndi chimodzi (6) la Ndime Yomanga, zambiri ziphunziridwa zanjira yomwe ikuchokera mu chitukuko cha mkati mwa mbumba ya moyo wapemphero wabwino – ndi kutumikira komwe imalimbikitsa – kufikira pa kuonekera kwa Nyumba Zikuluzikulu Zopemphereramo. Zokambirana zikuyambika ndi maBungwe Aakulu Auzimu, ndipo pomwe kukupitilira, tizilengeza pafupi-pafupi malo kumene Nyumba Yopembedzera yachiBaha’i yamangidwa mu zaka zikubwerazi.

Chimwemwe chathu powona mbumba ya Dzina Lalikulu ikulimbitsidwa chikumasokonezeka ndi chisoni chathu chachikulu powona kupitilira kwa mavuto ndi kulimbana padziko zomwe zikumabweretsa chisoni ndi kuvutika kwakulu – maka, powona kubadwanso kwa mphamvu zowononga zimene zasokoneza maubale a maiko pomwenso zoopsa zazikulu zikuchitikira makamu a anthu. Tikudziwa bwino lomwe ndipo tili wotsimikiziridwa kuti, ngati mbumba zachiBahá’í zaonetsa mobwereza-bwereza munjira zosiyana-siyana, otsatira a Bahá’u’lláh ndi odzipereka pa ntchito yochepetsa kuzunzika ndi kuthandiza iwo amene awazungulira, posatengera momwe iwo eni alili. Koma pokha-pokha mtundu wa anthu onse uchilimika kukhazikitsa ntchito zake pa maziko a chilungamo ndi choona, izi, Kalanga, zitha kubweretsa masautso opitilira. Tikupemphera kuti, ngati kuyambika kwa nkhondo posachedwapa kumaiko a azungu (Europe) kungabweretse maphunziro alionse pazatsogolo, idzatumikira ngati Chikumbutso pa mbali imene dziko liyenera kutenga ngati likufuna kupeza mtendere weni-weni ndi wopitilira. Mfundo zimene zinanenedwa ndi Baha’u’llah ku mafumu ndi mapulezidenti a nthawi Yake, ndi maudindo aakulu amene Iye anapereka kwa olamulira kalelo ndi panopa, tsopano utha kuoneka kufunika kwake lero kusiyana ndipo unalembedwa poyamba ndi Cholembera Chake. Kwa aBahá’í, kupita patsogolo mosakayika kwa Pulani Yayikulu ya Mulungu – kubwera pamodzi ndi mayesero ndi zosokoneza, koma mapeto ake kumema mtundu wa anthu ku chilungamo, mtendere, ndi mgwirizano – ndimomwe Pulani Yaying’ono ya Mulungu, imene okhulupilira atangwanika nayo kwakukulu, ikutambasukira. Kusalongosoka kwa zinthu m’tsiku lalero kukupangitsa kufunika kotulutsa mphamvu yomanga dera ya Chipembedzo kumveka mokwanira ndi motsindika.

Sitingayembekezere zina, pakali pano, koma kupitilira kwa kusokonezeka ndi kutekeseka kwa dziko; inu mosakayika muyamikira, choncho, kuti mpofunika kuti kupemphera koona mtima kulikonse komwe tikupereka kwa ana onse a Mulungu kuti amasulidwe mu mazunzo owawa ndikophatikizanso ndi pemphero la pansi pamtima pa kupita patsogolo kwa kutumikira komwe kukufunika panopa komwe mukupereka ku Chipembedzo cha Kalonga wa Mtendere.

Mu kalasita ina iliyonse zochita-chita za Pulani zayamba kupita patsogolo, tikuona kutukuka kwa mbumba ndi makhalidwe otamandika omwe tinafotokoza mu uthenga wamu 30 Disembala 2021. pomwe madera akukumana ndi mavuto a mitundu yosiyana-siyana, otsatira a Wokongola Wakumwamba ayenera kusiyana ndi ena pa makhalidwe awo a kupilira ndi nzeru, pa machitidwe awo ndi kutsatira mfundo, ndi kukhala a chifundo, odzipatula, ndi kulolerana komwe akuonetsa pofuna-funa mgwirizano. Nthawi ndi nthawi, makhalidwe opatulika ndi mchitidwe omwe okhulupilira akuonetsa mu nyengo zovuta kwambirizi zapangitsa anthu kutembenukira kwa aBaha’i pofuna chifotokozo, malangizo, ndi thandizo, maka pomwe moyo wa dera wasokonezeka ndi zosokoneza zosakonzekera. Pogawana izi, tikukumbukira kuti mbumba yachiBahá’í payokha nayonso ikukumana ndi zotsatira za mphamvu zowononga zimenezi zomwe zikugwira ntchito padziko lonse. Kuonjezera apo, tikuzindikira kuti kukula kwa kuyesetsa kwa abwenzi potukura Liu la Mulungu kupitilira, ndipomwenso akumane ndi mphamvu zolepheretsa, posakhalitsa kapena mtsogolo, kuchokera mbali zosiyana-siyana. Iwo ayenera kulimbitsa maganizo ndi mizimu yawo ku mayesero omwe abwera ndithu, kuti izi zisakhale zobwezeretsa m’mbuyo ntchito zawo. Koma okhulupilira akudziwa bwino lomwe kuti zovuta zina zilizonse zomwe zili mtsogolo mwawo, bwato la Chipembedzo ndilofana ndi iwo onse. Ndime zotsatana za ulendo wake zakumana ndi nyengo zimenezi ndipo zadutsa mafunde ake. Tsopano zikulunjika panjira yatsopano. Zitsimikizo za Wamphamvu Yonse ndi mweya umene ukuzaza paulendo wake ndikuyingolera iyo ku mapeto aulendo wake. Ndipo Pangano ndi nyenyezi yachitsogozo, kuonesetsa kuti bwato lili panjira yake yeni-yeni. Tipempha ochezera alendo akumwamba atumize madalitso awo pa onse omwe ali paulendo umenewu.

 

Windows / Mac