The Universal House of Justice
Ridván 2025
To the Bahá’ís of the World
Dearly loved Friends,
Inde, patangotsala chaka chimodzi kuti tikwangule ndime yoyamba ya Ndondomeko ya Zaka Zisanu ndi Zinayi, ndife okondwa kupereka tsatane-tsatane wa momwe ndondomekoyi ikuyendera—kubzolera m’zitsanzo zowala za kuyesetsa kwangwiro, zomwe Chipembedzochi chikuperekera masomphenya ndikudzadza mitima yochuluka ndi chiyembekezo.
Ndondomeko ya kukula ikupitira kupita patsogolo. Kubooleza kooneka kwachitika m’malo osiyana-siyana, kumene sikunachitikepo m’mbuyomu, komwe mbewu ya Chipembedzo tsopano yapatsa nthambi zatsopano zanthete ndipo kuthekera kogwira ntchito ndi mizimu yochuluka nthawi imodzi kwayamba kuwoneka. Kupita patsogolo uku kukutheka chifukwa cha mapayoniya odzipereka amene, ndimitima yoyatsidwa ndichikondi cha Mbuye wawo, achita machawi kukatumikira kwawo ngakhalenso kumaiko ena mwaunyinji ochititsa kaso. M’mikwamba momwe ndondomeko ya kukula inayamba kale, chidwi chatsopano chapatsidwa pa kugwiritsa ntchito, mwaluso ndi ukadaulo, njira zomwe zodziwika ndi m’ndandanda wa zochita zimene zipangitse abwenzi kudutsa mtunda wachiwiri ndi wachitatu. Ndipo mikwamba yamphamvu zoonekeratu, chithunzi champhamvu chomanga dera chachiChipembedzo chayamba kuoneka, pomwe patani yamphamvu ndi yosintha ya moyo wachiBahá’í ikuwonekera mu chiwerengero chochuluka cha mizimu yotsisimutsidwa.
Padakali pano, kukambirana ndi magulu am’dera kwapita patsogolo. Ntchito zam’madera zokhuza maphunziro zachulukana mofulumira kwambiri, komanso ntchito zina zapitanso patsogolo, monga zaulimi, zaumoyo, zachilengedwe, zopereka mphamvu kwa amayi komanso zaluso. Kupita patsogolo uku kukuwoneka kwambiri m’mikwamba yamphamvu kwambiri, kumene mudzi kapena dera—ngakhale m’ndandanda wa nyumba zingapo zondondozana kapena nyumba zakathithi—ndi kwawo kwa gulu lomwe likuona kutukuka komwe kumadza pakuyika mfundo zaChipembedzo muchikhalidwe chawo. M’malo ena, atsogoleri a dera pamodzi ndi iwo amene ali ndi udindo owona zamaphunziro a wana kapena chitukuko cham’dera sakungobwera kwa aBahá’í kuzafunsa nzeru kokha, koma akumafunanso kugwilira limodzi ntchito pofuna kupeza mayankho othekera. Kuwonjezera apo, ndife osangalala kuwona kuti pamlingo wadera komanso wadziko lonse, kachitidwe ndi kaganizidwe kachiBahá’í ku zokambirana zina zofunikira kukufuya kusililidwa ndi kuganiziridwa.
Chikonzero cha Zaka Zisanu ndi Zinayi chikudalira ndithu, pandondomeko ya dziko yophunzira zimene zili zopindulitsa m’madera aku Bolivia monga kuliri madera ena aku Sydney. Ndondomeko yakuphunzilirayi yabweretsa njira ndi machitidwe ogwirizana ndi dera lina lililonse. Ndiyadongosolo; ndiyosakakamiza; ndiyaponse-ponse. Ikubweretsa kulumikizana, kodzetsa maubale osiyana-siyana, pakati pa mawanja, pakati paokhala mowandikana, pakati pa achinyamata, komanso pakati pa onse omwe akonzeka kukhala atenga mbali mu ntchito yonyaditsayi. Imawutsa mbumba zosefukira ndikuthekera. Imalora kukwaniritsa maloto apamwamba omwe anthu omwe anasiyanitsidwa ndi malo, chiyankhulo, chikhalidwe, kapena zinthu zina koma tsopano amva ndi kuvomera kuyitana kwa Bahá’u’lláh kwa aliyense kuti “tiyesetse mosalekeza kutukula miyoyo ya wina ndi mnzake”. Ndipo zikudalira kotheratu pakuthekera kosalekeza kwa Liu la Mulungu— “mphamvu yoluzanitsa” ija, “yosuntha mizimu ndi yakuluzanitsa ndikubweretsa dongosolo m’dziko la umunthu”—ndipo pantchito yopitilira imapereka chilimbikitso.
Muchifwirimbiti cha thambo la m’dima, tawonani kuwala kothwanima kukuchokera mu kuyesesa kwakudzipereka kwanu! Ngakhale mkwiyo ukutsotsomoka m’dzikoli, thambo lomwe lidzakute mtundu wa anthu likumangidwa m’maiko, m’zigawo, ndi m’mikwamba. Koma zofunika kuchita ndizambiri. Mbumba iliyonse yam’dziko ili ndi chiyembekezo chake pakupita patsogolo komwe kukuyenera kuchitike mu ndime iyi, ndime yotsegulira Chikonzerochi. Nthawi ikupita. Abwenzi okondedwa, ndi ofalisa ziphunzitso zoyera, ndi achipambano a Wokongola Wodalitsika—kuyesetsa kwanu kukufunika pano. Kupita patsogolo kulikonse kumene kungachitike m'miyezi yolunjika ku Rizwáni akubwerayu kudzapereka mangolomera ku mbumba ya Dzina Lalikulu ku zimene iyenera kukwaniritsa mu ndime yachiwiri ya Chikonzerochi. Mulandire chipambano. Pa ichi tikupempha Ambuye wokwezeka; pa ichi tikupempha thandizo Lake losalephera; pa ichi tipemha Ambuye atumize angelo Ake okondedwa kuti athandize aliyense wa inu.
- The Universal House of Justice