Return   Facebook

The Universal House of Justice

Ridván 2020

To the Bahá’ís of the World

Dearly loved Friends,

Nkhani ziwiri zomwe zangochitika zatipangitsa ife kuti tigawane nanu mawu awa. Nkhani yoyamba ndi yokhudza mliri woopsa ndi osowetsa mtendere wa Corona omwe wakolera padziko lonse lapansi. Mmaiko ambiri, pambali pa kuyesetsa ndi khama kwa anthu limodzi kulimbana ndi vutoli, zotsatira zafika kale pachiopsezo, ndipo maanja ndi anthu akhudzidwa ndipo dziko lili pa mavuto. Mafunde a mazunzo ndi chisoni akufalikira dera ndi dera, ndipo izi zifooketsa maiko osiyana-siyana, pa nthawi zosiyana, munjira zosiyana-siyananso.

Nkhani yachiwiri, yomwe tsiku ndi tsiku ikuonekera, ndi kulimba mtima ndi kuchilimika kwa dziko lachiBaha’i mu nthawi ya msautsoyi yomwe sitingayifanirize ndi chilichonse. Kuyesetsa kwanu kwakhala kwa pamwamba. Pomwe tinakulemberani mwezi wapitawo pa Naw-Ruz, tinali ndi chidwi kutsindika za makhalidwe abwino omwe mbumba zomwe patani yawo ya kachitidwe kazinthu inasokonekera, zikuonetsa. Zonsezi zapangitsa mu sabata zotsatira, zimene abwenzi ochuluka anali kutsatira malamuo okhwima oyikidwa, kuzamitsa chiyamikiro chathu. Kuphunzira kochokera mbali zina za dziko lonse, mbumba zina zapeza njira zotetezeka ndi zabwino zobweretsa chidziwitso pa nkhani zaumoyo zofunikira kuzidziwa. Chidwi chachikulu chikuperekedwa kwa omwe ali pachiopsezo chachikulu ku nthendayi ndi zovuta zobwera ndi kufalikira kwa kachilomboka maka pankhani za chuma; kuyesetsa komwe akuchita ofalitsa nkhani pa makina a intaneti a Nkhani zokhudza a Baha’i padziko lonse (Baha’i World News Service) ndi chitsanzo chimodzi chabe mwa zambiri zomwe zili mkati. Izi zikuthandizidwa ndi kuyesetsa kopanga kafuku-fuku, kutukula ndi kubweretsa pamodzi makhalidwe auzimu amene ali ofunikira panthawi ino. Kuyesetsa kochuluka kotere kukuchitika pa banja kapena pawekha, koma pomwe pali kuthekera ndipo kulumikizana ndi kotheka, khalidwe lothandizana ndi kubwera pamodzi likupititsidwa patsogolo pakati pa anthu omwe ali mu vuto lofanana. Moyo wotaka-taka wa mbumba, ofunika kwambiri pa kupita patsogolo kwa dera sulepheretsedwa.

Mizimu yathu yalimbikitsidwa poona momwe maBungwe Auzimu Aakulu mothekera, atsogoleri a Wankhondo wa Kuwala atsogolera mbumba ndi kuthandiza kukonzekera bwino kuchitapo kanthu pa vutoli. Iwo athandizidwa molimba ndi Alangizi ndi Athandizi awo amene, monga mwa nthawi zonse, awonetsa moonadi mtima mlingo wa kutumikira mwachikondi. Pomwe akukhala odziwitsidwa bwino za kusintha komwe kukuchitika mmaiko awo, Mabungwe akonza zonse zofunikira zokhudza ntchito za kayendetsedwe ka Chipembedzo, maka pa nkhani ya masankho, ku malo komwe kuli ndi kuthekera. Kudzera mu kulumikizana kwapafupi-fupi, zikhazikitso ndi makomiti apereka ulangizi wanzeru, kupereka chitsimikizo ndi chilimbikitso pafupi-pafupi. Nthawi zambiri, ayambanso kufufuza mfundo zomanga zimene zikuyamba kuonekera mu zochitika za m’madera. Chiyembekezo chimene tidapereka mu uthenga wathu wa Naw-Ruz kuti mayesero awa akupilira kwa mtundu wa anthu adzapereka kuzindikira kwakukulu kwayamba kale kuoneka. Atsogoleri, anthu oganiza bwino ndi opereka malipoti ayamba kufufuza mfundo zokhazikika ndi zokhumba zachindunji kuti, mu nthawi ya posachedwa, zakhala zikusowa kwambiri mu ntchito zam’dera. Mu nthawi ino izi zilingati kuthwanima koyambilira, komabe zikuonetsa kuthekera kuti nthawi ya kukhudzika kwa pamodzi kutha kukhala kwayandikira.

Mtidzi omwe tili nawo poona kuchilimika kwa dziko la chiBaha’i pochita ntchito kukusokonezeka ndi chisoni pa zotsatira za mliri wu pa mtundu wa anthu. Kalanga! Tikuzindikira kuti okhulupilira ndi abwenzi awo akumvanso kusautsidwa kotere. Kupatukana kwa abwenzi ndi abale kumene, potsatira zofunikira poziteteza, anthu ambiri mu dziko lapansi tsopano akusunga chifuniro, kwa ena, kupereka njira ku kusiyana kwa muyaya. Tsiku lililonse kukuoneka kuti ululu wochuluka uzikhalapo dzuwa lisanalowe. Tipempha lonjezo la kulumikizananso mu ulemelero wosatha kupereka chilimbikitso kwa iwo amene ataya okondedwa awo. Tikupemphera kuti mitima yawo ipepukidwe, ndi chisomo cha Mulungu chizungulire iwo amene maphunziro awo, ntchito, m’makomo awo, ngakhalenso zowalora kupitilira pa moyo zili pa chiopsezo. Kwa inu, ndi iwo amene tikuwanyadira ndi abwenzi onse, tipempha kwa Baha’u’llah ndi kufufuza madalitso ndi chisomo Chake.

Ungatalike ndi kuvuta bwanji mseu umene tiyenera kuyendamo, tili ndi chikhulupiliro chapamwamba pa kulimba mtima ndi kuchilimika kwanu pa ulendo umenewu. Mukutengako kuchokera mu nkhokwe ya chiyembekezo, chikhulupiliro ndi kuganiza kwapamwamba, kuyika zofuna za ena patsogolo pa zofuna zanu, kulora iwo amene amanidwa chakudya chauzimu, iwo amene ali ndi ludzu lopeza mayankho kuti akhale okhutitsidwa, ndi iwo amene ali ndi khumbo lofuna kutumikira ku ubwino wa dziko lapansi kuti apatsidwe zoyenelera. Kuchokera kwa otsatira odzipereka a Wolungama Wodalitsika, tingayembekeze bwanji zochepa?

 

Windows / Mac