Bahá'í Prayers

Chichewa : UMODZI

Permanent Link

 

O Mulungu wanga! O Mulungu wanga! Lumikizani mitima ya antchito Anu, ndipo Muwaululire iwo cholinga Chanu Chachikulu. Aloleni iwo atsate malangizo Anu ndi kusunga malamulo Anu. Athandizeni iwo, O Mulungu, mukuyesetsa kwao, ndipo muwapatse mphamvu kuti akutumikireni Inu. O Mulungu, Musawasiye iwo mwa iwo okha, koma mutsogoze mapazi awo ndi kuwala kwa nzeru Zanu ndipo sangalatsani mitima yawo ndi chikondi Chanu. Indetu, Inu Ndinu Mthandizi wawo ndi Mbuye wawo.

 

Permanent Link

 

Mulungu lolani kuti kuwala kwa mgwirizano kukutire dziko lonse lapansi, ndi chizindikiro chakuti “Ufumu ngwa Mulungu” chisindikizidwe pamphumi pa anthu Ake onse.

 

Permanent Link

 

Ulemelero ukhale kwa Inu, O Mulungu, chifukwa chakuwonetsa chikondi Chanu kwa mtundu wa anthu! O Inu Amene Muli Moyo wathu ndi Kuwunika kwathu, tsogolereni a ntchito Anu mu njira Yanu, ndipo mutipatse kukhala wolemera mwa Inu ndi kukhala omasuka ku ziri zonse kupatula Inu Nokha.

O Mulungu, Tiphunzitseni Umodzi Wanu ndipo Mutipatse kuzindikira Mgwirizano Wanu, kuti tisawone aliyense koma Inu Nokha. Inu Ndinu Wachifundo ndi Wopatsa Chaulere. O Mulungu, Lengani m’mitima ya wokondeka Anu moto wa chikondi Chanu, kuti utenthe maganizo a chirichonse kupatula a Inu Nokha.

Tiululireni, O Mulungu, Ukulu Wanu wosatha-kuti Inu mudalipo ndipo mudzakhalapobe nthawi zonse, ndipo kuti kulibenso Mulungu wina koma Inu Nokha. Indetu, mwa Inu tidzapeza chitonthozo ndi mphamvu.

 

Windows / Mac