O Mulungu wanga! O Mulungu wanga! Lumikizani mitima ya antchito Anu, ndipo Muwaululire iwo cholinga Chanu Chachikulu. Aloleni iwo atsate malangizo Anu ndi kusunga malamulo Anu. Athandizeni iwo, O Mulungu, mukuyesetsa kwao, ndipo muwapatse mphamvu kuti akutumikireni Inu. O Mulungu, Musawasiye iwo mwa iwo okha, koma mutsogoze mapazi awo ndi kuwala kwa nzeru Zanu ndipo sangalatsani mitima yawo ndi chikondi Chanu. Indetu, Inu Ndinu Mthandizi wawo ndi Mbuye wawo.
- Bahá'u'lláh
Mulungu lolani kuti kuwala kwa mgwirizano kukutire dziko lonse lapansi, ndi chizindikiro chakuti “Ufumu ngwa Mulungu” chisindikizidwe pamphumi pa anthu Ake onse.
- Bahá'u'lláh
Ulemelero ukhale kwa Inu, O Mulungu, chifukwa chakuwonetsa chikondi Chanu kwa mtundu wa anthu! O Inu Amene Muli Moyo wathu ndi Kuwunika kwathu, tsogolereni a ntchito Anu mu njira Yanu, ndipo mutipatse kukhala wolemera mwa Inu ndi kukhala omasuka ku ziri zonse kupatula Inu Nokha.
O Mulungu, Tiphunzitseni Umodzi Wanu ndipo Mutipatse kuzindikira Mgwirizano Wanu, kuti tisawone aliyense koma Inu Nokha. Inu Ndinu Wachifundo ndi Wopatsa Chaulere. O Mulungu, Lengani m’mitima ya wokondeka Anu moto wa chikondi Chanu, kuti utenthe maganizo a chirichonse kupatula a Inu Nokha.
Tiululireni, O Mulungu, Ukulu Wanu wosatha-kuti Inu mudalipo ndipo mudzakhalapobe nthawi zonse, ndipo kuti kulibenso Mulungu wina koma Inu Nokha. Indetu, mwa Inu tidzapeza chitonthozo ndi mphamvu.
- Bahá'u'lláh